< Yona 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
And the word of the Lord was maad to Jonas,
2 “Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
sone of Amathi, and seide, Rise thou, and go in to Nynyue, the greet citee, and preche thou ther ynne, for the malice therof stieth vp bifore me.
3 Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
And Jonas roos for to fle in to Tharsis, fro the face of the Lord. And he cam doun to Joppe, and foond a schip goynge in to Tharsis, and he yaf schip hire to hem; and he wente doun in to it, for to go with hem in to Tharsis, fro the face of the Lord.
4 Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
Forsothe the Lord sente a greet wynd in the see, and a greet tempest was maad in the see, and the schip was in perel for to be al to-brokun.
5 Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
And schip men dredden, and men crieden to her god; and senten vessels, that weren in the schip, in to the see, that it were maad liytere of hem. And Jonas wente doun in to the ynnere thingis of the schip, and slepte bi a greuouse sleep.
6 Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
And the gouernour cam to him, and seide to hym, Whi art thou cast doun in sleep? rise thou, clepe thi God to help, if perauenture God ayenthenke of vs, and we perische not.
7 Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
And a man seide to his felowe, Come ye, and caste we lottis, and wite we, whi this yuel is to vs. And thei kesten lottis, and lot felle on Jonas.
8 Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
And thei seiden to hym, Schewe thou to vs, for cause of what thing this yuel is to vs; what is thi werk, which is thi lond, and whidur goist thou, ether of what puple art thou?
9 Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
And he seide to hem, Y am an Ebrew, and Y drede the Lord God of heuene, that made the see and the drie lond.
10 Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
And the men dredden with greet drede, and seiden to him, Whi didist thou this thing? for the men knewen that he flei fro the face of the Lord, for Jonas hadde schewide to hem.
11 Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
And thei seiden to hym, What schulen we do to thee, and the see schal seesse fro vs? for the see wente, and wexe greet on hem.
12 Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
And he seide to hem, Take ye me, and throwe in to the see, and the see schal ceesse fro you; for Y woot, that for me this greet tempest is on you.
13 Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
And men rowiden, for to turne ayen to the drie lond, and thei miyten not, for the see wente, and wexe greet on hem.
14 Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
And thei crieden to the Lord, and seiden, Lord, we bisechen, that we perische not in the lijf of this man, and that thou yyue not on vs innocent blood; for thou, Lord, didist as thou woldist.
15 Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
And thei token Jonas, and threwen in to the see; and the see stood of his buylyng.
16 Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
And the men dredden the Lord with greet drede, and offriden oostis to the Lord, and vowiden avowis.
17 Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.
And the Lord made redi a greet fisch, that he shulde swolowe Jonas; and Jonas was in the wombe of the fisch thre daies and thre niytis.

< Yona 1 >