< Yona 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
And the word of the Lord came to Jonah the son of Amittai, saying:
2 “Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
Rise and go to Nineveh, the great city, and preach in it. For its malice has ascended before my eyes.
3 Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
And Jonah rose in order to flee from the face of the Lord to Tarshish. And he went down to Joppa and found a ship bound for Tarshish. And he paid its fare, and he went down into it, in order to go with them to Tarshish from the face of the Lord.
4 Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
But the Lord sent a great wind into the sea. And a great tempest took place in the sea, and the ship was in danger of being crushed.
5 Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
And the mariners were afraid, and the men cried out to their god. And they threw the containers that were in the ship into the sea in order to lighten it of them. And Jonah went down into the interior of the ship, and he fell into a painful deep sleep.
6 Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
And the helmsman approached him, and he said to him, “Why are you weighed down with sleep? Rise, call upon your God, so perhaps God will be mindful of us and we might not perish.”
7 Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
And a man said to his shipmate, “Come, and let us cast lots, so that we may know why this disaster is upon us.” And they cast lots, and the lot fell upon Jonah.
8 Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
And they said to him: “Explain to us what is the reason that this disaster is upon us. What is your work? Which is your country? And where are you going? Or which people are you from?”
9 Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
And he said to them, “I am Hebrew, and I fear the Lord God of heaven, who made the sea and the dry land.”
10 Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
And the men were greatly afraid, and they said to him, “Why have you done this?” (For the men knew that he was fleeing from the face of the Lord, because he had told them.)
11 Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
And they said to him, “What are we to do with you, so that the sea will cease for us?” For the sea flowed and swelled.
12 Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
And he said to them, “Take me, and cast me into the sea, and the sea will cease for you. For I know that it is because of me that this great tempest has come upon you.”
13 Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
And the men were rowing, so as to return to dry land, but they did not succeed. For the sea flowed and swelled against them.
14 Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
And they cried out to the Lord, and they said, “We beseech you, Lord, do not let us perish for this man’s life, and do not attribute to us innocent blood. For you, Lord, have done just as it pleased you.”
15 Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
And they took Jonah and cast him into the sea. And the sea was stilled from its fury.
16 Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
And the men feared the Lord greatly, and they sacrificed victims to the Lord, and they made vows.
17 Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.
And the Lord prepared a great fish to swallow Jonah. And Jonah was in the belly of the fish for three days and three nights.

< Yona 1 >