< Yohane 8 >

1 Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
mais Jésus s'est rendu sur le mont des Oliviers.
2 Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
Or, de grand matin, il entra de nouveau dans le temple, et tout le peuple vint à lui. Il s'assit et les enseigna.
3 Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
Les scribes et les pharisiens amenèrent une femme surprise en adultère. L'ayant placée au milieu,
4 anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
ils lui dirent: Maître, nous avons trouvé cette femme adultère, en flagrant délit.
5 Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
Or, dans notre loi, Moïse nous a ordonné de lapider de telles femmes. Que dis-tu donc d'elle? »
6 Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
Ils dirent cela pour l'éprouver, afin d'avoir quelque chose à lui reprocher. Mais Jésus se baissa et écrivit sur la terre avec son doigt.
7 Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
Comme ils continuaient à l'interroger, il leva les yeux et leur dit: « Que celui d'entre vous qui est sans péché lui jette la première pierre. »
8 Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
De nouveau, il se baissa et écrivit sur la terre avec son doigt.
9 Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
Ceux-ci, après avoir entendu cela, convaincus par leur conscience, sortirent un par un, depuis le plus âgé jusqu'au dernier. Jésus resta seul avec la femme, là où elle était, au milieu.
10 Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
Jésus, s'étant levé, la vit et dit: « Femme, où sont tes accusateurs? Personne ne t'a condamnée? »
11 Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
Elle a dit: « Personne, Seigneur. » Jésus a dit: « Je ne te condamne pas non plus. Va ton chemin. Désormais, ne pèche plus. »
12 Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
Jésus leur parla de nouveau, en disant: « Je suis la lumière du monde. Celui qui me suit ne marchera pas dans les ténèbres, mais il aura la lumière de la vie. »
13 Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
Les pharisiens lui dirent donc: « Tu témoignes de toi-même. Ton témoignage n'est pas valable. »
14 Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
Jésus leur répondit: « Même si je rends témoignage de moi-même, mon témoignage est vrai, car je sais d'où je viens et où je vais; mais vous, vous ne savez ni d'où je viens ni où je vais.
15 Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
Vous jugez selon la chair. Moi, je ne juge personne.
16 Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
Et quand bien même je jugerais, mon jugement est vrai, car je ne suis pas seul, mais je suis avec le Père qui m'a envoyé.
17 Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
Il est aussi écrit dans votre loi que le témoignage de deux personnes est valable.
18 Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
Moi, je suis celui qui rend témoignage de moi-même, et le Père qui m'a envoyé rend témoignage de moi. »
19 Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
Ils lui dirent donc: « Où est ton Père? » Jésus répondit: « Vous ne connaissez ni moi ni mon Père. Si vous me connaissiez, vous connaîtriez aussi mon Père. »
20 Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
Jésus prononça ces paroles dans le trésor, comme il enseignait dans le temple. Et personne ne l'arrêta, parce que son heure n'était pas encore venue.
21 Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
Jésus leur dit donc encore: « Je m'en vais, et vous me chercherez, et vous mourrez dans vos péchés. Là où je vais, vous ne pouvez pas venir. »
22 Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
Les Juifs dirent donc: « Se tuera-t-il, parce qu'il dit: « Où je vais, vous ne pouvez pas venir »? »
23 Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
Il leur dit: « Vous êtes d'en bas. Moi, je suis d'en haut. Vous êtes de ce monde. Je ne suis pas de ce monde.
24 Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
Je vous ai donc dit que vous mourrez dans vos péchés; car si vous ne croyez pas que je suis lui, vous mourrez dans vos péchés. »
25 Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
Ils lui dirent donc: « Qui es-tu? » Jésus leur dit: « Ce que je vous dis depuis le commencement.
26 ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
J'ai beaucoup de choses à dire et à juger à votre sujet. Mais celui qui m'a envoyé est vrai; et ce que j'ai entendu de lui, je le dis au monde entier. »
27 Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
Ils ne comprenaient pas qu'il leur parlait du Père.
28 Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
Jésus leur dit donc: « Quand vous aurez élevé le Fils de l'homme, vous saurez que c'est moi, et je ne fais rien de moi-même; mais c'est comme mon Père me l'a enseigné que je dis ces choses.
29 Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
Celui qui m'a envoyé est avec moi. Le Père ne m'a pas laissé seul, car je fais toujours ce qui lui est agréable. »
30 Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
Comme il parlait ainsi, beaucoup crurent en lui.
31 Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
Jésus dit donc aux Juifs qui avaient cru en lui: « Si vous demeurez dans ma parole, vous êtes vraiment mes disciples.
32 Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
Vous connaîtrez la vérité, et la vérité vous rendra libres. »
33 Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
Ils lui répondirent: « Nous sommes la descendance d'Abraham, et nous n'avons jamais été asservis à personne. Comment peux-tu dire: « Vous serez libérés »? »
34 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
Jésus leur répondit: Je vous le dis en vérité, quiconque commet un péché est esclave du péché.
35 Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn g165)
Un esclave ne demeure pas toujours dans la maison. Un fils demeure pour toujours. (aiōn g165)
36 Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
Si donc le Fils vous rend libres, vous serez vraiment libres.
37 Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
Je sais que vous êtes la postérité d'Abraham, et pourtant vous cherchez à me tuer, parce que ma parole ne trouve pas de place en vous.
38 Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
Je dis les choses que j'ai vues avec mon Père; et vous aussi, vous faites les choses que vous avez vues avec votre père. »
39 Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
Ils lui répondirent: « Notre père est Abraham. » Jésus leur dit: « Si vous étiez les enfants d'Abraham, vous feriez les œuvres d'Abraham.
40 Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
Mais maintenant vous cherchez à me tuer, moi qui vous ai dit la vérité que j'ai entendue de Dieu. Ce n'est pas Abraham qui a fait cela.
41 Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
Vous faites les œuvres de votre père. » Ils lui dirent: « Nous ne sommes pas nés de l'immoralité sexuelle. Nous avons un seul Père, Dieu. »
42 Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
C'est pourquoi Jésus leur dit: « Si Dieu était votre père, vous m'aimeriez, car je suis sorti et je suis venu de Dieu. Car je ne suis pas venu de moi-même, mais c'est lui qui m'a envoyé.
43 Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
Pourquoi ne comprenez-vous pas ma parole? Parce que vous n'entendez pas ma parole.
44 Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
Vous êtes de votre père le diable, et vous voulez faire les désirs de votre père. Il a été meurtrier dès le commencement, et il ne tient pas dans la vérité, parce qu'il n'y a pas de vérité en lui. Quand il dit un mensonge, il parle de lui-même, car il est menteur et père du mensonge.
45 Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
Mais parce que je dis la vérité, vous ne me croyez pas.
46 Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
Lequel d'entre vous me convainc de péché? Si je dis la vérité, pourquoi ne me croyez-vous pas?
47 Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
Celui qui est de Dieu entend les paroles de Dieu. C'est pourquoi vous n'entendez pas, parce que vous n'êtes pas de Dieu. »
48 Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
Alors les Juifs lui répondirent: « Ne disons-nous pas bien que tu es un Samaritain, et que tu as un démon? »
49 Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
Jésus répondit: « Je n'ai pas de démon, mais j'honore mon Père et vous me déshonorez.
50 Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
Mais je ne cherche pas ma propre gloire. Il y a quelqu'un qui cherche et qui juge.
51 Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn g165)
En vérité, je vous le dis, si quelqu'un garde ma parole, il ne verra jamais la mort. » (aiōn g165)
52 Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn g165)
Alors les Juifs lui dirent: « Nous savons maintenant que tu as un démon. Abraham est mort, ainsi que les prophètes; et toi, tu dis: « Si quelqu'un garde ma parole, il ne goûtera jamais à la mort. (aiōn g165)
53 Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
Es-tu plus grand que notre père Abraham, qui est mort? Les prophètes sont morts. Pour qui te prends-tu? »
54 Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
Jésus répondit: « Si je me glorifie moi-même, ma gloire n'est rien. C'est mon Père qui me glorifie, lui dont vous dites qu'il est notre Dieu.
55 Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
Vous ne l'avez pas connu, mais moi, je le connais. Si je disais: « Je ne le connais pas », je serais comme vous, un menteur. Mais moi, je le connais et je garde sa parole.
56 Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
Ton père Abraham s'est réjoui de voir mon jour. Il l'a vu et s'est réjoui. »
57 Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
Les Juifs lui dirent donc: « Tu n'as pas encore cinquante ans! As-tu vu Abraham? »
58 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
Jésus leur dit: « En vérité, je vous le dis, avant qu'Abraham n'existe, JE SUIS. »
59 Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.
Ils prirent donc des pierres pour les jeter contre lui, mais Jésus se cacha et sortit du temple, après avoir traversé le milieu d'eux, et il passa ainsi.

< Yohane 8 >