< Yohane 17 >

1 Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera: “Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu.
Kinuna ni Jesus dagitoy a banbanag, kalpasanna ket intangadna dagiti matana iti langlangit ket kinunana, “Ama, dimtengen ti oras; padayawam toy Anak mo tapno ti Anak padayawan na ka—
2 Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. (aiōnios g166)
a kas iti panangtedmo kenkuana ti turay kadagiti amin a lasag tapno mangted isuna ti biag nga agnanayon kadagiti amin nga intedmo kenkuana. (aiōnios g166)
3 Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. (aiōnios g166)
Daytoy ti biag nga agnanayon: a maam-ammodaka, ti maymaysa a pudno a Dios, ken kenkuana nga isu iti imbaonmo, ni Jesu-Cristo. (aiōnios g166)
4 Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire.
Indaydayawka ditoy daga, naturposko ti trabaho nga intedmo kaniak nga aramidek.
5 Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.
Ita, Ama, padayawannak dita biangmo iti dayag nga adda kaniak idi addaak kenka dita dennam sakbay a naparsua ti lubong.
6 “Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu.
Impakaammok ti naganmo kadagiti tattao nga intedmo kaniak a nagtaud iti lubong. Kukuam ida; ket intedmo ida kaniak, ken sinalimetmetanda ti saom.
7 Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu.
Ita ammoda nga aniaman a banbanag nga inted mo kaniak ket nagtaudda kenka,
8 Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine.
ta dagiti sao nga inted mo kaniak— intedko dagitoy a sasao kadakuada. Inawatda dagitoy ken pudno nga ammoda a nagtaudak kenka, ket namatida nga imbaonnak.
9 Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu.
Agkararagak para kadakuada, saanak nga agkarkararag para iti lubong ngem kadagiti intedmo kaniak, ta kukuam ida.
10 Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo.
Amin a banbanag a kukuak ket kukuam, ken amin a banbanag a kukuam ket kukuak; maidaydayawak kadakuada.
11 Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
Awanakon iti lubong, ngem addada dagitoy a tattao iti lubong ket umayakon kenka. Nasantoan nga Ama, pagtalinaedem ida iti naganmo nga intedmo kaniak tapno agbalinda a maymaysa, a kas kadata a maymaysa.
12 Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.
Bayat iti kaaddaak kadakuada, sinalimetmetak ida iti naganmo nga intedmo kaniak; inaywanak ida, ket awan kadakuada iti uray maysa a napukaw, malaksid ti anak iti pannakadadael, tapno ti kasta matungpal dagiti sursurat.
13 “Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo.
Itan umayakon kenka; ngem ibagbagak dagitoy a banbanag iti lubong tapno iti kasta maipaay kadakuada ti rag-ok a naananay.
14 Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
Intedko kadakuada ti saom; ginura ida ti lubong gapu ta saanda a taga-lubong, a kas kaniak a saan a taga-lubong.
15 Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo.
Saanko nga ikararag a masapul nga alaem ida manipud ditoy lubong ngem masapul nga iyadayom ida manipud iti maysa a dakes.
16 Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi.
Saanda a taga lubong a kas kaniak a saan a taga lubong.
17 Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi.
Idatonmo ida kenka iti kinapudno, ta ti saom ket kinapudno.
18 Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi.
Imbaonnak iti lubong, ket imbaonko ida iti lubong.
19 Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.
Maipaay iti pagimbaganda indatonko ti bagik kenka tapno maidatonda met dagiti bagbagida kenka iti kinapudno.
20 “Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo.
Saanko laeng nga ikarkararag dagitoy, ngem uray pay dagiti asinoman a mamati kaniak babaen iti saoda,
21 Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine.
tapno mabalinda amin iti agmaymaysa, uray a kas kenka, Ama, addaka kaniak, ket addaak kenka. Ikararagko pay nga addada met kadata tapno mamati ti lubong nga imbaonnak.
22 Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi.
Ti dayag nga intedmo kaniak—intedko kadakuada, tapno kasta agmaymaysada, a kas met kadata a maymaysa-
23 Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.
Addaak kadakuada, ken addaka kaniak, tapno agbalinda a naan-anay iti panagmaymaysa; iti kasta maammoan ti lubong nga imbaonnak, ken inayatmo ida, a kas iti panangayatmo kaniak.
24 “Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.
Ama, dagidiay nga intedmo kaniak— Tarigagayak pay nga addada kaniak no sadino ti ayanko tapno makitada ti dayagko, nga intedmo kaniak: ta inayatnak manipud pay idi sakbay iti pannakabangon ti lubong.
25 “Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine.
Nalinteg nga Ama, saannaka nga am-ammo ti lubong, ngem am-ammoka; ken ammo dagitoy nga imbaonnak.
26 Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”
Impakaammok ti naganmo kadakuada, ket ipakaammok daytoy tapno ti ayat a panangayatmo kaniak ket adda koma kadakuada, ket addaak kadakuada.”

< Yohane 17 >