< Machitidwe a Atumwi 1 >
1 Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
Ti immuna a libro nga insuratko, O Teofilo, imbagana amin dagiti inrugi ni Jesus nga aramiden ken isuro,
2 mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
agingga iti aldaw a naawat isuna sadiay ngato. Daytoy ket kalpasan nga intedna ti bilin babaen iti Espiritu Santo kadagiti pinilina nga apostol, nga isu dagiti nagparanganna a sibibiag
3 Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
kalpasan iti panagsagsagabana. Iti uppat a pulo nga al-aldaw, intultuloyna ti nagparang kadakuada, nangibagbaga kadagiti banbanag a maipanggep iti pagarian ti Dios.
4 Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
Idi nakisinnarak isuna kadakuada, imbilinna a saanda a panawan ti Jerusalem, ngem urayenda ti kari iti Ama, a kinunana, “Nangngegyo manipud kaniak
5 Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
a pudno unay a nangbautisar ni Juan babaen iti danum, ngem mabautisarankayto babaen iti Espiritu Santo, iti mabiit.”
6 Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
Idi naummongda, sinaludsodda kenkuana, “Apo, daytoy kadin ti tiempo nga isublim ti pagarian iti Israel?”
7 Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
Kinunana kadakuada, “Saan a para kadakayo ti mangammo iti tiempo wenno iti panawen nga inkeddeng ti Ama babaen iti bukodna a turay.
8 Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
Ngem umawatkayonto iti pannakabalin, inton umay kadakayo ti Espiritu Santo, ket dakayonto dagiti saksik idiay Jerusalem ken iti amin a Judea ken Samaria, ken kadagiti sulsuli ti daga.”
9 Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
Idi naibagan ni Apo Jesus dagitoy a banbanag, bayat a kumitkitada sadiay ngato, naipangato isuna, ket inlemmeng isuna iti ulep manipud kadagiti matada.
10 Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
Kabayatan iti napinget a panangkitada iti langit bayat a mapmapan isuna, kellaat nga adda dua a lallaki a nakapuraw a nakatakder ti abayda.
11 Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
Kinunada, “Dakayo a lallaki iti Galilea, apay a nakatakder kayo ditoy a kumitkita idiay langit? Daytoy Jesus a nagpangato idiay langit ket agsublinto iti wagas a kas metlaeng iti nakitayo a pannakaipangatona sadi langit.”
12 Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
Kalpasanna, nagsublida idiay Jerusalem manipud idiay Bantay ti Olibo, nga asideg iti Jerusalem, a madalliasat iti kas kapaut ti Aldaw a Panaginana.
13 Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
Idi nakasangpetdan, napanda iti akin-ngato a siled, nga isu iti pagigiananda. Isuda da Pedro, Juan, Santiago, Andres, Felipe, Tomas, Bartolome, Mateo, Santiago nga anak ni Alfeo, Simon a Patriota, ken Judas nga anak ni Santiago.
14 Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
Sangsangkamaysada amin a sipapasnek a nangitultuloy iti panagkararag. Ket karaman ditoy dagiti babbai, ni Maria nga ina ni Jesus, ken dagiti kakabsat ni Jesus a lallaki.
15 Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
Kadagidiay nga al-aldaw, timmakder ni Pedro iti nagtetengngaan dagiti kakabsat, agarup sangagasut ket duapulo a tattao, ket kinunana,
16 Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
“Kakabsat, nasisita a matungpal ti Nasantoan a Surat, nga insaksakbay nga insao ti Espiritu Santo babaen iti ngiwat ni David maipapan kenni Judas, nga isu iti nangidaulo kadagiti nangtiliw kenni Jesus.
17 Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
Ta maysa met isuna kadatayo ken inawatna ti bingayna kadagiti pagnumaran iti daytoy a ministerio.”
18 (Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
(Tatta, daytoy a lalaki ket nakagatang iti taltalon babaen iti birok ti dakes nga aramidna. Kalpasanna, natinnag nga umuna ti ulona, ken bimtak ti bagina, ket amin a lalaem iti tianna ket naiburais.
19 Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
Naammoan daytoy dagiti amin nga agnanaed idiay Jerusalem, isu nga iti bukodda a pagsasao, inawaganda dayta a taltalon iti “Akeldama,” dayta ket, “Kataltalunan ti Dara.”)
20 Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
Ta naisurat iti Libro dagiti Salmo, 'Mabaybay-an koma dagiti taltalonna, ken awan koma ti uray a tao nga agnaed sadiay'; ken, 'Maipasublat koma iti sabali ti takemna a kinamangidadaulo.'
21 Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
Nasisita ngarud, a maysa kadagiti lallaki a kimmuykuyog kadatayo iti amin a tiempo a kaadda ni Apo Jesus kadatayo,
22 kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
manipud idi nangrugi a nangbautisar ni Juan agingga iti aldaw a naala ni Jesus manipud kadatayo, masapul a kaduatayo a saksi iti panagungarna.”
23 Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
Impasangoda dagiti dua a lallaki, ni Jose a maawagan Barsabas, a managan met laeng iti Justo, ken ni Matias.
24 Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
Nagkararagda ket kinunada, “Sika, Apo, ammom ti adda iti puspuso iti amin a tattao, isu nga ipaltiingmo koma no siasino kadagitoy a dua ti napilim
25 kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
a mangsublat iti akem iti daytoy a ministerio ken kinaapostol a linabsing ni Judas iti ipapanna iti bukodna a lugar.”
26 Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.
Binunotda no siasino kadakuada ti napili ket nabunot ni Matias. Ket naibilang isuna kadagiti sangapulo ket maysa nga apostol.