< Yohane 1 >

1 Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
Au commencement était la Parole, et la Parole était avec Dieu, et la Parole était Dieu.
2 Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
Le même était au commencement avec Dieu.
3 Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
Toutes choses ont été faites par elle. Sans elle, rien n'a été fait de ce qui a été fait.
4 Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
En lui était la vie, et la vie était la lumière des hommes.
5 Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
La lumière brille dans les ténèbres, et les ténèbres ne l'ont pas vaincue.
6 Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
Il vint un homme envoyé de Dieu, dont le nom était Jean.
7 Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
Il est venu comme témoin, afin de rendre témoignage à la lumière, pour que tous croient par lui.
8 Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
Il n'était pas la lumière, mais il a été envoyé pour rendre témoignage à la lumière.
9 Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
La vraie lumière, qui éclaire tout le monde, venait dans le monde.
10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
Il était dans le monde, et le monde a été fait par lui, et le monde ne l'a pas reconnu.
11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
Il est venu vers les siens, et les siens ne l'ont pas reçu.
12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
Mais à tous ceux qui l'ont reçu, il a donné le droit de devenir enfants de Dieu, à ceux qui croient en son nom,
13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
lesquels sont nés, non du sang, ni de la volonté de la chair, ni de la volonté de l'homme, mais de Dieu.
14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
Le Verbe s'est fait chair et a vécu parmi nous. Nous avons vu sa gloire, une gloire comme celle du Fils unique du Père, plein de grâce et de vérité.
15 Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
Jean rendit témoignage de lui. Il s'est écrié: « C'est celui dont j'ai dit: Celui qui vient après moi m'a surpassé, car il était avant moi. »
16 Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
De sa plénitude, nous avons tous reçu grâce sur grâce.
17 Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
Car la loi a été donnée par Moïse. La grâce et la vérité ont été réalisées par Jésus-Christ.
18 Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
En aucun temps, personne n'a vu Dieu. Le Fils unique, qui est dans le sein du Père, l'a déclaré.
19 Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
Tel est le témoignage de Jean, lorsque les Juifs envoyèrent de Jérusalem des prêtres et des lévites pour lui demander: « Qui es-tu? »
20 Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
Il a déclaré, et n'a pas nié, mais il a déclaré: « Je ne suis pas le Christ. »
21 Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
Ils lui demandèrent: « Qui donc? Es-tu Élie? » Il a dit: « Je ne le suis pas. » « Vous êtes le prophète? » Il a répondu: « Non. »
22 Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
Ils lui dirent donc: « Qui es-tu? Donne-nous une réponse à rapporter à ceux qui nous ont envoyés. Que dis-tu de toi-même? »
23 Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
Il dit: « Je suis la voix de celui qui crie dans le désert: « Aplanissez le chemin du Seigneur », comme l'a dit le prophète Ésaïe. »
24 Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
Ceux qui avaient été envoyés étaient des pharisiens.
25 anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
Ils lui demandèrent: « Pourquoi donc baptises-tu, si tu n'es ni le Christ, ni Élie, ni le prophète? »
26 Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
Jean leur répondit: « Moi, je baptise dans l'eau, mais il y a parmi vous quelqu'un que vous ne connaissez pas.
27 Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
C'est lui qui vient après moi, qui est préféré à moi, et dont je ne suis pas digne de délier la courroie de la sandale. »
28 Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
Ces choses se passaient à Béthanie, de l'autre côté du Jourdain, où Jean baptisait.
29 Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
Le lendemain, il vit Jésus venir à lui, et il dit: « Voici l'Agneau de Dieu, qui enlève le péché du monde!
30 Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
C'est lui dont j'ai dit: « Après moi vient un homme qui est préféré à moi, car il était avant moi.
31 Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
Je ne l'ai pas connu, mais c'est pour cela que je suis venu baptiser dans l'eau, afin qu'il soit révélé à Israël. »
32 Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
Jean rendit ce témoignage: « J'ai vu l'Esprit descendre du ciel comme une colombe, et il est resté sur lui.
33 Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
Je ne l'ai pas reconnu, mais celui qui m'a envoyé baptiser dans l'eau m'a dit: « Celui sur qui tu verras l'Esprit descendre et rester, c'est celui qui baptise dans l'Esprit Saint.
34 Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
J'ai vu et j'ai témoigné que c'est le Fils de Dieu. »
35 Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
Le lendemain, Jean se tenait encore debout avec deux de ses disciples,
36 Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
et, regardant Jésus qui marchait, il dit: « Voici l'Agneau de Dieu. »
37 Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
Les deux disciples l'entendirent parler, et ils suivirent Jésus.
38 Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
Jésus se retourna, les vit qui le suivaient, et leur dit: « Que cherchez-vous? » Ils lui dirent: « Rabbi » (ce qui veut dire, en étant interprété, Maître), « où demeures-tu? »
39 Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
Il leur dit: « Venez et voyez. » Ils sont venus et ont vu où il se trouvait, et ils sont restés avec lui ce jour-là. C'était environ la dixième heure.
40 Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
L'un de ceux qui avaient entendu Jean et qui le suivirent était André, frère de Simon Pierre.
41 Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
Il trouva d'abord son propre frère, Simon, et lui dit: « Nous avons trouvé le Messie! » (c'est-à-dire, selon l'interprétation, le Christ).
42 Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
Il l'amena à Jésus. Jésus le regarda et dit: « Tu es Simon, fils de Jonas. On t'appellera Céphas » (ce qui est, par interprétation, Pierre).
43 Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
Le lendemain, décidé à aller en Galilée, il trouva Philippe. Jésus lui dit: « Suis-moi. »
44 Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
Or, Philippe était de Bethsaïda, la ville d'André et de Pierre.
45 Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
Philippe, ayant trouvé Nathanaël, lui dit: « Nous avons trouvé celui dont Moïse, dans la loi, et aussi les prophètes, ont parlé: Jésus de Nazareth, fils de Joseph. »
46 Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
Nathanaël lui dit: « Peut-il sortir quelque chose de bon de Nazareth? » Philippe lui dit: « Viens et vois. »
47 Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
Jésus, voyant Nathanaël s'approcher de lui, dit à son sujet: « Voici vraiment un Israélite en qui il n'y a aucune tromperie! »
48 Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
Nathanaël lui dit: « Comment me connais-tu? » Jésus lui répondit: « Avant que Philippe ne t'appelle, quand tu étais sous le figuier, je t'ai vu. »
49 Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
Nathanaël lui répondit: « Rabbi, tu es le Fils de Dieu! Tu es le Roi d'Israël! »
50 Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
Jésus lui répondit: « Parce que je t'ai dit: « Je t'ai vu sous le figuier », crois-tu? Tu verras des choses plus grandes que celles-ci! »
51 Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”
Il lui dit: « Très certainement, je vous le dis à tous, vous verrez désormais le ciel ouvert, et les anges de Dieu monter et descendre sur le Fils de l'homme. »

< Yohane 1 >