< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
A word of YHWH that has been to Joel, son of Pethuel:
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear this, you aged ones, And give ear, all you inhabitants of the land, Has this been in your days? Or in the days of your fathers?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Concerning it talk to your sons, And your sons to their sons, And their sons to another generation.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
What is left of the palmer-worm, the locust has eaten, And what is left of the locust, The cankerworm has eaten, And what is left of the cankerworm, The caterpillar has eaten.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake, you drunkards, and weep, And howl all drinking wine, because of the juice, For it has been cut off from your mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a nation has come up on My land, Strong, and there is no number, Its teeth [are] the teeth of a lion, And it has the jaw-teeth of a lioness.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
It has made My vine become a desolation, And My fig tree become a splinter, It has made it thoroughly bare, and has cast down, Its branches have been made white.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Wail, as a virgin girds with sackcloth, For the husband of her youth.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
Present and drink-offering have been cut off from the house of YHWH, The priests have mourned, servants of YHWH.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
The field is spoiled, The ground has mourned, For the grain is spoiled, New wine has been dried up, oil languishes.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Be ashamed, you farmers, Howl, vinedressers, for wheat and for barley, For the harvest of the field has perished.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine has been dried up, And the fig tree languishes, Pomegranate, also palm, and apple-tree, All trees of the field have withered, For joy has been dried up from the sons of men.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Gird, and lament, you priests, Howl, you servants of the altar, Come in, lodge in sackcloth, servants of my God, For present and drink-offering have been withheld from the house of your God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Sanctify a fast, proclaim a restraint, Gather [the] elderly [and] all those inhabiting the land, [Into the] house of your God YHWH,
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
And cry to YHWH, “Aah! For the day! For [the] Day of YHWH [is] near, And it comes as destruction from [the] Almighty.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Is food not cut off before our eyes? Joy and rejoicing from the house of our God?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
Scattered things have rotted under their clods, Storehouses have been desolated, Granaries have been broken down, For the grain has withered.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
How livestock have sighed! Perplexed have been droves of oxen, For there is no pasture for them, Also droves of sheep have been desolated.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
To You, O YHWH, I call, For fire has consumed lovely places of a wilderness, And a flame has set on fire all trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Also the livestock of the field long for You, For dried up have been streams of water, And fire has consumed lovely places of a wilderness!”

< Yoweli 1 >