< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
A word of YHWH that has been to Hosea, son of Beeri, in the days of Uzziah, Jotham, Ahaz, Hezekiah, kings of Judah, and in the days of Jeroboam son of Joash, king of Israel:
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
The commencement of YHWH’s speaking by Hosea. And YHWH says to Hosea, “Go, take a woman of whoredoms for yourself, and children of whoredoms, for the land goes utterly whoring from after YHWH.”
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
And he goes and takes Gomer daughter of Diblaim, and she conceives and bears a son to him;
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
and YHWH says to him, “Call his name Jezreel, for yet a little, and I have charged the blood of Jezreel on the house of Jehu, and have caused the kingdom of the house of Israel to cease;
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
and it has come to pass in that day that I have broken the bow of Israel in the Valley of Jezreel.”
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
And she conceives again, and bears a daughter, and He says to him, “Call her name Lo-Ruhamah [(Not Loved)], for I no longer pity the house of Israel, for I utterly take them away;
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
and I pity the house of Judah, and have saved them by their God YHWH, and do not save them by bow, and by sword, and by battle, by horses, and by horsemen.”
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
And she weans Lo-Ruhamah, and conceives, and bears a son;
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
and He says, “Call his name Lo-Ammi [(Not My People)], for you [are] not My people, and I am not for you;
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
and the number of the sons of Israel has been as the sand of the sea that is not measured nor numbered, and it has come to pass in the place where it is said to them, You [are] not My people, it is said to them, Sons of the Living God;
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
and the sons of Judah and the sons of Israel have been gathered together, and they have appointed one head for themselves, and have gone up from the land, for great [is] the day of Jezreel.”

< Hoseya 1 >