< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
Herrens Ord, som kom til Joel, Pethuels Søn.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hører dette, I gamle! og laaner Øren, alle Landets Indbyggere! mon saadant er sket i eders Dage eller i eders Fædres Dage?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Fortæller eders Børn derom, og eders Børn fortælle deres Børn og deres Børn den næste Slægt!
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
Hvad Høskrækken lod overblive, aad Græshoppen, og hvad Græshoppen lod overblive, aad Oldenborren, og hvad Oldenborren lod overblive, aad Kornormen.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Vaagner op, I drukne, og græder! og hyler, alle I, som drikke Vin, over Mosten! thi den er reven bort fra eders Mund.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
Thi et Folk er draget op over mit Land, stærkt og ikke til at tælle; det har Tænder som Løvers Tænder og Kindtænder som Løvindens.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
Det har ødelagt mit Vintræ og knækket mit Figentræ; det har gjort det aldeles bart og kastet det ned, Rankerne derpaa ere blevne hvide.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Hyl som en Jomfru, der har iført sig Sæk for sin Ungdoms Brudgom!
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
Madoffer og Drikoffer er revet bort for Herrens Hus, Præsterne, Herrens Tjenere, sørge.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
Marken er ødelagt, Jordbunden sørger; thi Kornet er ødelagt, Mosten er fortørret, Olien er sygnet hen.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Agerdyrkerne ere beskæmmede, Vingaardsmændene hyle over Hveden og over Bygget; thi Høsten paa Marken er gaaet tabt.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
Vintræet er fortørret, og Figentræet er sygnet hen; Granatæbletræet, selv Palmetræet og Æbletræet, alle Træer paa Marken ere fortørrede; ja, Fryd er skamfuld vegen bort fra Menneskenes Børn.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Omgjorder eder og sørger, I Præster! hyler, I Altertjenere! gaar ind, tilbringer Natten i Sørgedragt, I min Guds Tjenere! thi Madoffer og Drikoffer er forment eders Guds Hus.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Helliger en Faste, udraaber en Forsamling, samler de Ældste, alle Landets Indbyggere til Herrens eders Guds Hus, og raaber til Herren!
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Ve, den Dag! thi Herrens Dag er nær og skal komme som en Ødelæggelse fra den Almægtige.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Er ikke Føden reven bort for vore Øjne, Glæde og Fryd fra vor Guds Hus?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
Sædekornene ere raadnede under Jordskorpen, Forraadshusene ligge øde, Laderne ere nedbrudte, fordi Kornet er blevet til Skamme.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
Hvor sukker dog Kvæget! Øksnenes Hjorde ere forvildede, thi de have ingen Græsgang, ogsaa Faarehjordene maa bøde.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
Til dig, Herre! vil jeg raabe; thi en Ild har fortæret Græsgangene i Ørken, og en Lue har svedet alle Træerne paa Marken.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Ogsaa Dyrene paa Marken se sukkende op til dig; thi Vandstrømmene ere udtørrede, og en Ild har fortæret Græsgangene i Ørken.

< Yoweli 1 >