< Yoweli 2 >

1 Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
Støder i Basunen paa Zion, og raaber højt paa mit hellige Bjerg, alle Landets Indbyggere bæve! thi Herrens Dag kommer, thi den er nær.
2 tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
En Mørkheds og Dunkelheds Dag, en Dag med Sky og Mulm, som Morgenrøde udbredt over Bjergene! et stort og mægtigt Folk, hvis Lige ikke har været fra Arilds Tid og ikke heller skal komme etter det, saa mange Aar der er Slægt efter Slægt til!
3 Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
Foran det fortærer en Ild, og efter det brænder en Lue; foran det er Landet som Edens Have, men efter det som en øde Ørk, og heller intet undslipper det.
4 Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
Dets Udseende er som Heste at se til, og som Rideheste saa rende de.
5 Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
De springe paa Bjergenes Toppe, med en Lyd som af Vogne, med en Lyd som af Ildslue, der fortærer Halm, som et mægtigt Folk, der er rustet til Krig.
6 Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
Folkene bæve for dets Ansigt, alle Ansigter skifte Farve.
7 Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
Som vældige komme de løbende, som Krigsmænd bestige de Muren; og de drage frem, hver sin Vej, og forandre ikke deres Retning.
8 Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
Og de trænge ikke den ene den anden, de drage frem, hver ad sin slagne Vej; og de styrte frem igennem Vaaben, de bryde ikke af.
9 Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
De løbe om i Staden, rende paa Muren, stige ind i Husene; de komme ind igennem Vinduerne som en Tyv.
10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
Foran dem bæver Jorden, Himmelen ryster; Sol og Maane sortne, og Stjerner drage deres Glans tilbage.
11 Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
Og Herren opløfter sin Røst foran sin Hær, thi saare stor er hans Lejr, thi mægtig er den, som udretter hans Ord; thi stor er Herrens Dag og saare forfærdelig, og hvo kan udholde den?
12 “Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
Og selv nu, siger Herren, vender om til mig af eders ganske Hjerte og med Faste og med Graad og med Klage,
13 Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
og sønderriver eders Hjerte, og ikke eders Klæder, og vender om til Herren, eders Gud; thi han er naadig og barmhjertig, langmodig og stor af Miskundhed og angrer det onde.
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
Hvo ved? han maatte maaske vende om og angre det, saa at han lader Velsignelse efter sig, Madoffer og Drikoffer for Herren, eders Gud.
15 Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
Støder i Basunen paa Zion, helliger en Faste, udraaber en Forsamling!
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
Samler Folket, helliger en Forsamling, sanker de gamle, samler de spæde Børn og dem, som die Brysterne; en Brudgom gaa ud af sit Kammer og en Brud af sit Brudehus!
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
Præsterne, Herrens Tjenere, skulle græde imellem Forhallen og Alteret, og de skulle sige: Herre! spar dit Folk og giv ikke din Arv hen til Skændsel, saa at Hedningerne skulle herske over dem; hvorfor skulle de sige iblandt Folkene: Hvor er deres Gud?
18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
Og Herren var nidkær for sit Land og sparede sit Folk.
19 Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
Og Herren svarede og sagde til sit Folk: Se, jeg sender eder Kornet og Mosten og Olien, og I skulle mættes dermed; og jeg vil ikke ydermere gøre eder til Spot iblandt Hedningerne.
20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
Og ham fra Norden vil jeg drive langt bort fra eder og støde ham ud i et tørt og øde Land, hans Fortrop imod det østre Hav og hans Bagtrop imod det vestre Hav; og der skal opstige en Stank af ham og opstige en væmmelig Lugt af ham; thi han tog sig for at gøre store Ting.
21 Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
Frygt ikke, du Jord! fryd dig og vær glad; thi Herren har taget sig for at gøre store Ting.
22 Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
Frygter ikke, I Dyr paa Marken! thi Græsgangene i Ørken grønnes; thi Træet bærer sin Frugt, Figentræerne og Vintræerne give deres Kraft.
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
Og I, Zions Børn! fryder og glæder eder i Herren eders Gud; thi han giver eder Læreren til Retfærdighed og nedsender saa til eder for det første tidlig Regn og sildig Regn.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
Og Tærskepladserne skulle være fulde af Korn og Persekarrene løbe over med Most og Olie.
25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
Og jeg vil godtgøre eder Aarene, i hvilke Græshoppen, Oldenborren og Kornormen og Høskrækken fortærede, denne min store Hær, som jeg havde sendt paa eder.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
Og I skulle æde, æde og mættes, og love Herrens eders Guds Navn, som har handlet underfuldt med eder, og mit Folk skal ikke beskæmmes evindelig.
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
Og I skulle fornemme, at jeg er midt i Israel, og jeg er Herren eders Gud, og ingen ydermere; og mit Folk skal ikke beskæmmes evindelig.
28 “Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
Og det skal ske derefter, at jeg vil udgyde min Aand over alt Kød, og eders Sønner og eders Døtre skulle profetere; eders Ældste skulle drømme Drømme og eders unge Karle se Syner.
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
Ogsaa over Tjenere og over Tjenestepiger vil jeg i de samme Dage udgyde min Aand.
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
Og jeg vil give underfulde Tegn paa Himmelen og paa Jorden, Blod og Ild og Røgstøtter.
31 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
Solen skal omvendes til Mørke og Maanen til Blod, førend Herrens Dag, den store og forfærdelige, kommer.
32 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.
Og det skal ske, at hver, som paakalder Herrens Navn, skal undkomme; thi paa Zions Bjerg og i Jerusalem skal der være nogle, som undkomme, saaledes som Herren har sagt, og iblandt de undslupne skal den være, som Herren kalder.

< Yoweli 2 >