< Yoweli 3 >

1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
Јер, гле, у оне дане и у оно време, кад вратим робље Јудино и јерусалимско,
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
Сабраћу све народе, и свешћу их у долину Јосафатову, и онде ћу се судити с њима за свој народ и за наследство своје Израиља, ког расејаше међу народе и разделише земљу моју;
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
И за мој народ бацаше жреб, и даваше дете за курву, и продаваше девојку за вино, те пише.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
И шта хоћете ви са мном, Тире и Сидоне, и сви крајеви палестински? Хоћете ли да ми платите? И хоћете ли да ми вратите? Одмах ћу вам без оклевања платити плату вашу на вашу главу.
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
Јер узесте сребро моје и злато моје, и најлепше закладе моје унесосте у своје цркве.
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
И синове Јудине и синове јерусалимске продадосте синовима грчким да бисте их отерали далеко од међе њихове.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Ево, ја ћу их дигнути с места куда их продадосте, и платићу вам плату вашу на вашу главу.
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
И продаћу ваше синове и ваше кћери у руке синовима Јудиним, и они ће их продати Савејцима у народ далеки, јер Господ рече.
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Објавите ово по народима, огласите рат, подигните јунаке нека дођу и иду сви војници.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Раскујте раонике своје на мачеве, и српове своје на копља; ко је слаб, нека рече: Јунак сам.
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Скупите се и ходите, сви народи унаоколо, и саберите се! Тамо сведи, Господе, јунаке своје.
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
Нека се подигну и дођу народи у долину Јосафатову; јер ћу онде сести да судим свим народима унаоколо.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Замахните српом, јер је жетва узрела; ходите, сиђите, јер је тесак пун, каце се преливају; јер је злоћа њихова велика.
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
Гомиле, гомиле у долини судској; јер је дан Господњи близу у долини судској.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
Сунце ће и месец помркнути, и звезде ће устегнути своју светлост.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
И Господ ће рикнути са Сиона, и из Јерусалима ће пустити глас свој, и затрешће се небо и земља; али ће Господ бити уточиште свом народу и крепост синовима Израиљевим.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
И познаћете да сам ја Господ Бог ваш, који наставам у Сиону, у светој гори својој; и Јерусалим ће бити свет, и туђинци неће више ићи по њему.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
И тада ће горе капати слатким вином, и хумови ће се топити од млека, и свим потоцима Јудиним тећи ће вода, и изаћи ће извор из дома Господњег и натопиће долину Ситим.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
Мисир ће опустети, и едомска ће бити пуста пустиња за насиље учињено синовима Јудиним, јер пролише крв праву у земљи њиховој.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
А Јуда ће стајати довека и Јерусалим од колена до колена.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
И очистићу крв њихову, које не очистих; и Господ ће наставати у Сиону.

< Yoweli 3 >