< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
Речи Амоса који беше између пастира из Текује, што виде за Израиља за времена Озије цара Јудиног и за времена Јеровоама сина Јоасовог цара Израиљевог, две године пре труса.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
Рече дакле: Господ ће рикнути са Сиона, и из Јерусалима ће пустити глас свој, и тужиће станови пастирски и посушиће се врх Кармилу.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Дамаск, нећу му опростити, јер врхоше Галад гвозденом браном.
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
Него ћу пустити огањ у дом Азаилов, те ће прождрети дворове Вен-Ададове.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
И поломићу преворнице Дамаску, и истребићу становнике из поља Авена, и оног који држи палицу из дома Еденовог, и отићи ће у ропство народ сирски у Кир, вели Господ.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Газа, нећу јој опростити, јер их заробише сасвим и предадоше Едомцима.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Него ћу пустити огањ у зидове Гази, те ће јој прождрети дворове.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
И истребићу становнике из Азота и оног који држи палицу из Аскалона, и окренућу руку своју на Акарон, и изгинуће остатак филистејски, вели Господ Господ.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Тир, нећу му опростити, јер сасвим дадоше у ропство Едомцима и не сећаше се братске вере.
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
Него ћу пустити огањ у зидове Тиру, те ће прождрети дворове његове.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Едом, нећу му опростити, јер гони брата свог мачем потрвши у себи све жаљење, и гнев његов раздире једнако, и срдњу своју држи увек.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
Него ћу пустити огањ у Теман, и прождреће дворе у Восори.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Овако вели Господ: За три зла и за четири што учинише синови Амонови, нећу им опростити, јер параше трудне жене у Галаду да рашире међу своју.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
Него ћу запалити огањ у зидовима Рави, те ће јој прождрети дворове с виком у дан боја и с буром у дан вихора.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
И цар ће њихов отићи у ропство, он и кнезови његови с њим, вели Господ.

< Amosi 1 >