< Yobu 39 >
1 “Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
Poznaš čas, ko divje skalne koze kotijo? Mar lahko zaznamuješ kdaj košute povržejo?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Mar lahko šteješ mesece, ki so jih dopolnile? Ali poznaš čas, ko kotijo?
3 Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
Sklonijo se in skotijo svoje mlade, odvržejo svoje bridkosti.
4 Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
Njihovi mladiči so v dobri naklonjenosti, rastejo z žitom, gredo naprej in se ne vrnejo k njim.
5 “Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
Kdo je divjega osla izpustil na prostost? Ali kdo je odvezal vezi divjega osla?
6 Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
Čigar hišo sem naredil divjino in jalovo deželo njegova prebivališča?
7 Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
Zasmehuje mestno množico niti se ne ozira na vpitje voznika.
8 Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
Razpon gora je njegov pašnik in preiskuje za vsako zeleno stvarjo.
9 “Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
Mar ti bo samorog voljan služiti, ali ostane pri tvojih jaslih?
10 Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
Ali lahko s svojim jermenom zvežeš samoroga v brazdo? Ali bo za teboj branal doline?
11 Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
Mu boš zaupal, ker je njegova moč velika? Ali boš svoje trdo delo prepustil njemu?
12 Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
Mu boš verjel, da bo tvoje seme pripeljal domov in ga zbral v tvoj skedenj?
13 “Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
Daješ pavom čedne peruti? Ali peruti in peresa noju?
14 Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
Ki zapušča svoja jajca na zemlji in jih ogreva v prahu
15 nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
in pozablja, da jih stopalo lahko zdrobi ali da jih divja žival lahko stre.
16 Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
Trda je do svojih malih, kakor da ne bi bili njeni. Brez strahu je, da je njeno trdo delo zaman,
17 Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
ker ji je Bog odrekel modrost niti ji ni podelil razumnosti.
18 Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
Ko se dvigne visoko, zasmehuje konja in njegovega jezdeca.
19 “Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
Si ti dal konju moč? Si ti njegov vrat oblekel z grivo?
20 Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
Ga lahko narediš prestrašenega kakor kobilico? Slava njegovih nosnic je strašna.
21 Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Grebe v dolini in se veseli v svoji moči. Gre naprej, da sreča oborožene ljudi.
22 Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
Zasmehuje strah in ni zgrožen niti se pred mečem ne obrača nazaj.
23 Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
Tul za puščice rožlja ob njem, lesketajoča sulica in ščit.
24 Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
Tla požira z okrutnostjo in besom. Niti ne verjame, da je to zvok šofarja.
25 Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
Med šofarji hrže: ›Hi, hi‹ in od daleč voha bitko, grmenje poveljnikov in bojni krik.
26 “Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
Mar sokol leti po svoji modrosti in svoje peruti razpenja proti jugu?
27 Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
Mar se orlica vzpenja ob tvoji zapovedi in svoje gnezdo dela na višini?
28 Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
Prebiva in ostaja na skali, na skalni pečini in trdnem kraju.
29 Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
Od tam si išče plen in njene oči zrejo daleč proč.
30 Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”
Tudi njeni mladiči srkajo kri. In kjer so umorjeni, tam je ona.«