< Yobu 3 >
1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
Después de esto abrió Job su boca, y maldijo su día.
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Perezca el día en que yo fui nacido, y la noche que dijo: Concebido es varón.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Aquel día fuera tinieblas, y Dios no curara de él desde arriba, ni claridad resplandeciera sobre él.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Ensuciáranle tinieblas y sombra de muerte; reposara sobre él nublado, que le hiciera horrible como día caluroso.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
A aquella noche ocupara oscuridad, ni fuera contada entre los días del año, ni viniera en el número de los meses.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Oh si fuera aquella noche solitaria, que no viniera en ella canción;
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Maldijéranla los que maldicen al día, los que se aparejan para levantar su llanto.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Las estrellas de su alba fueran oscurecidas; esperara la luz, y no viniera; ni viera los párpados de la mañana.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
Porque no cerró las puertas del vientre donde yo estaba, ni escondió de mis ojos la miseria.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
¿Por qué no morí yo desde la matriz, y fui traspasado en saliendo del vientre?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
¿Por qué me previnieron las rodillas, y para qué los pechos que mamase?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Porque ahora yaciera y reposara; durmiera, y entonces tuviera reposo,
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
Con los reyes, y con los consejeros de la tierra, que edifican para sí los desiertos;
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
O con los príncipes que poseen el oro, que hinchen sus casas de plata.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
O ¿ por qué no fui escondido como abortivo, como los pequeñitos que nunca vieron luz?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Allí los impíos dejaron el miedo, y allí descansaron los de cansadas fuerzas.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
Allí también reposaron los cautivos, no oyeron la voz del exactor.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
Allí está el chico y el grande: allí es el siervo libre de su señor.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
¿Por qué dio luz al trabajado, y vida a los amargos de ánimo?
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
Que esperan la muerte, y no la hay: y la buscan más que tesoros.
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
Que se alegran de grande alegría, y se gozan cuando hallan el sepulcro.
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
Al hombre que no sabe por donde vaya, y que Dios le encerró.
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
Porque antes que mi pan, viene mi suspiro: y mis gemidos corren como aguas.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
Porque el temor que me espantaba, me ha venido, y háme acontecido lo que temía.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Nunca tuve paz, nunca me sosegué, ni nunca me reposé; y vínome turbación.