< Yobu 8 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Y respondió Baldad Sujita, y dijo:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
¿Hasta cuándo hablarás esto, y las palabras de tu boca serán como un viento fuerte?
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
¿Si pervertirá Dios el derecho, y si el Todopoderoso pervertirá la justicia?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Si tus hijos pecaron contra él, él los echó en el lugar de su pecado.
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
Si tú de mañana buscares a Dios, y rogares al Todopoderoso:
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Si fueres limpio y derecho, cierto luego se despertará sobre ti, y hará próspera la morada de tu justicia:
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
De tal manera que tu principio habrá sido pequeño en comparación del grande crecimiento de tu postrimería.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Porque pregunta ahora a la edad pasada, y dispónte para inquirir de sus padres de ellos;
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
Porque nosotros somos desde ayer, no sabemos, siendo nuestros días sobre la tierra como sombra.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
¿No te enseñarán ellos, te dirán, y de su corazón sacarán estas palabras?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
¿El junco crece sin cieno? ¿crece el prado sin agua?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
¿Aun él en su verdura no será cortado, y antes de toda yerba se secará?
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Tales son los caminos de todos los que olvidan a Dios; y la esperanza del impío perecerá.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Porque su esperanza será cortada, y su confianza es casa de araña.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
El estribará sobre su casa, mas no permanecerá en pie: recostarse ha sobre ella, mas no se afirmará.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Un árbol está verde delante del sol, y sus renuevos salen sobre su huerto:
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
Junto a una fuente sus raíces se van entretejiendo, y enlazándose hasta un lugar pedregoso.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Si le arrancaren de su lugar, y negare de él, diciendo: Nunca te vi:
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Ciertamente este será el gozo de su camino; y de la tierra de donde se traspusiére retoñecerán otros.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
He aquí, Dios no aborrece al perfecto, ni toma la mano de los malignos.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Aun henchirá tu boca de risa, y tus labios de jubilación.
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Los que te aborrecen, serán vestidos de confusión; y la habitación de los impíos perecerá.