< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
Post haec aperuit Iob os suum, et maledixit diei suo,
2 Ndipo Yobu anati:
et locutus est.
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Pereat dies in qua natus sum, et nox in qua dictum est: Conceptus est homo.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Dies ille vertatur in tenebras, non requirat eum Deus desuper, et non illustretur lumine.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Obscurent eum tenebrae et umbra mortis, occupet eum caligo, et involvatur amaritudine.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Noctem illam tenebrosus turbo possideat, non computetur in diebus anni, nec numeretur in mensibus:
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Sit nox illa solitaria, nec laude digna:
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Maledicant ei qui maledicunt diei, qui parati sunt suscitare Leviathan:
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Obtenebrentur stellae caligine eius: expectet lucem et non videat, nec ortum surgentis aurorae:
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
Quia non conclusit ostia ventris, qui portavit me, nec abstulit mala ab oculis meis.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
Quare non in vulva mortuus sum, egressus ex utero non statim perii?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
Quare exceptus genibus? cur lactatus uberibus?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Nunc enim dormiens silerem, et somno meo requiescerem:
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
Cum regibus et consulibus terrae, qui aedificant sibi solitudines:
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
Aut cum principibus, qui possident aurum, et replent domos suas argento:
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
Aut sicut abortivum absconditum non subsisterem, vel qui concepti non viderunt lucem.
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Ibi impii cessaverunt a tumultu, et ibi requieverunt fessi robore.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
Et quondam vincti pariter sine molestia, non audierunt vocem exactoris.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
Parvus et magnus ibi sunt, et servus liber a domino suo.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
Quare misero data est lux, et vita his, qui in amaritudine animae sunt?
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
qui expectant mortem, et non venit, quasi effodientes thesaurum:
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
Gaudentque vehementer cum invenerint sepulchrum.
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
Viro cuius abscondita est via, et circumdedit eum Deus tenebris?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
Antequam comedam suspiro: et tamquam inundantes aquae, sic rugitus meus:
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
Quia timor, quem timebam, evenit mihi: et quod verebar accidit.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Nonne dissimulavi? nonne silui? nonne quievi? et venit super me indignatio.

< Yobu 3 >