< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Et respondens Iob, ait:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Vere scio quod ita sit, et quod non iustificetur homo compositus Deo.
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Si voluerit contendere cum eo, non poterit ei respondere unum pro mille.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Sapiens corde est, et fortis robore: quis restitit ei, et pacem habuit?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Qui transtulit montes, et nescierunt hi quos subvertit in furore suo.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Qui commovet terram de loco suo, et columnae eius concutiuntur.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Qui praecipit Soli, et non oritur: et stellas claudit quasi sub signaculo:
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Qui extendit caelos solus, et graditur super fluctus maris.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Qui facit Arcturum, et Oriona, et Hyadas, et interiora austri.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Qui facit magna, et incomprehensibilia, et mirabilia, quorum non est numerus.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Si venerit ad me, non videbo eum: si abierit, non intelligam.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Si repente interroget, quis respondebit ei? vel quis dicere potest: Cur ita facis?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Deus, cuius irae nemo resistere potest, et sub quo curvantur qui portant orbem.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Quantus ergo sum ego, ut respondeam ei, et loquar verbis meis cum eo?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Qui etiam si habuero quippiam iustum, non respondebo, sed meum iudicem deprecabor.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Et cum invocantem exaudierit me, non credo quod audierit vocem meam.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
In turbine enim conteret me, et multiplicabit vulnera mea etiam sine causa.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Non concedit requiescere spiritum meum, et implet me amaritudinibus.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Si fortitudo quaeritur, robustissimus est: si aequitas iudicii, nemo audet pro me testimonium dicere.
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Si iustificare me voluero, os meum condemnabit me: si innocentem ostendero, pravum me comprobabit.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Etiam si simplex fuero, hoc ipsum ignorabit anima mea, et taedebit me vitae meae.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Unum est quod locutus sum, et innocentem et impium ipse consumit.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Si flagellat, occidat semel, et non de poenis innocentum rideat.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Terra data est in manus impii, vultum iudicum eius operit: quod si non ille est, quis ergo est?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Dies mei velociores fuerunt cursore: fugerunt, et non viderunt bonum.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Pertransierunt quasi naves poma portantes, sicut aquila volans ad escam.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Cum dixero: Nequaquam ita loquar: commuto faciem meam, et dolore torqueor.
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Verebar omnia opera mea, sciens quod non parceres delinquenti.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Si autem et sic impius sum, quare frustra laboravi?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Si lotus fuero quasi aquis nivis, et fulserint velut mundissimae manus meae:
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Tamen sordibus intinges me, et abominabuntur me vestimenta mea.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Neque enim viro qui similis mei est, respondebo: nec qui mecum in iudicio ex aequo possit audiri.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Non est qui utrumque valeat arguere, et ponere manum suam in ambobus.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Auferat a me virgam suam, et pavor eius non me terreat.
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Loquar, et non timebo eum: neque enim possum metuens respondere.

< Yobu 9 >