< Yobu 22 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Então respondeu Eliphaz o temanita, e disse:
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Porventura o homem será de algum proveito a Deus? antes a si mesmo o prudente será proveitoso.
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Ou tem o Todo-poderoso prazer em que tu sejas justo? ou lucro algum que tu faças perfeitos os teus caminhos?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Ou te repreende, pelo temor que tem de ti? ou entra contigo em juízo?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Porventura não é grande a tua malícia? e sem termo as tuas iniquidades?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Porque penhoraste a teus irmãos sem causa alguma, e aos nus despiste os vestidos.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Não deste de beber água ao cançado, e ao faminto retiveste o pão.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Mas para o violento era a terra, e o homem tido em respeito habitava nela.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
As viúvas despediste vazias, e os braços dos órfãos foram quebrantados.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Por isso é que estás cercado de laços, e te perturbou um pavor repentino,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Ou as trevas que não vês, e a abundância d'água que te cobre.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Porventura Deus não está na altura dos céus? olha pois para o cume das estrelas, quão levantadas estão.
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
E dizes que sabe Deus disto? porventura julgará por entre a escuridão?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
As nuvens são escondedura para ele, para que não veja: e passeia pelo circuito dos céus.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Porventura consideraste a vereda do século passado, que pisaram os homens iníquos?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Os quais foram arrebatados antes do seu tempo: sobre cujo fundamento um dilúvio se derramou.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Diziam a Deus: Retira-te de nós. E que é o que o Todo-poderoso lhes fez?
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Sendo ele o que enchera de bens as suas casas: mas o conselho dos ímpios esteja longe de mim.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
Os justos o viram, e se alegravam, e o inocente escarneceu deles.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Porquanto o nosso estado não foi destruído, mas o fogo consumiu o resto deles.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Acostuma-te pois a ele, e tem paz, e assim te sobrevirá o bem.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Aceita, peço-te, a lei da sua boca, e põe as suas palavras no teu coração.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
Se te converteres ao Todo-poderoso, serás edificado: afasta a iniquidade da tua tenda.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Então amontoarás ouro como pó, e o ouro de Ophir como pedras dos ribeiros.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
E até o Todo-poderoso te será por ouro, e a tua prata amontoada.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
Porque então te deleitarás no Todo-poderoso, e levantarás o teu rosto para Deus.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Deveras orarás, a ele, e ele te ouvirá, e pagarás os teus votos.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Determinando tu algum negócio, ser-te-á firme, e a luz brilhará em teus caminhos.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
Quando abaterem, então tu dirás: Haja exaltação: e Deus salvará ao humilde.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
E livrará até ao que não é inocente; porque fica livre pela pureza de tuas mãos.