< Yobu 22 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Then Eliphaz the Temanite answered and said,
2 “Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Can a man be profitable unto El, as he that is wise may be profitable unto himself?
3 Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
Is it any pleasure to the Almighty, that thou art righteous? or is it gain to him that thou makest thy ways perfect?
4 “Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Will he reprove thee for fear of thee? will he enter with thee into judgment?
5 Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
Is not thy wickedness great? and thine iniquities infinite?
6 Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
For thou hast taken a pledge from thy brother for nought, and stripped the naked of their clothing.
7 Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
Thou hast not given water to the weary to drink, and thou hast withholden bread from the hungry.
8 ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
But as for the mighty man, he had the earth; and the honourable man dwelt in it.
9 Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
Thou has sent widows away empty, and the arms of the fatherless have been broken.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
Therefore snares are round about thee, and sudden fear troubleth thee;
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
Or darkness, that thou canst not see; and abundance of waters cover thee.
12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
Is not Eloah in the height of heaven? and behold the height of the stars, how high they are!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
And thou sayest, How doth El know? can he judge through the dark cloud?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
Thick clouds are a covering to him, that he seeth not; and he walketh in the circuit of heaven.
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
Hast thou marked the old way which wicked men have trodden?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
Which were cut down out of time, whose foundation was overflown with a flood:
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
Which said unto El, Depart from us: and what can the Almighty do for them?
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
Yet he filled their houses with good things: but the counsel of the wicked is far from me.
19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
The righteous see it, and are glad: and the innocent laugh them to scorn.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
Whereas our substance is not cut down, but the remnant of them the fire consumeth.
21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
Acquaint now thyself with him, and be at peace: thereby good shall come unto thee.
22 Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
Receive, I pray thee, the law from his mouth, and lay up his words in thine heart.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
If thou return to the Almighty, thou shalt be built up, thou shalt put away iniquity far from thy tabernacles.
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
Then shalt thou lay up gold as dust, and the gold of Ophir as the stones of the brooks.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
Yea, the Almighty shall be thy defence, and thou shalt have plenty of silver.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
For then shalt thou have thy delight in the Almighty, and shalt lift up thy face unto Eloah.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
Thou shalt make thy prayer unto him, and he shall hear thee, and thou shalt pay thy vows.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
Thou shalt also decree a thing, and it shall be established unto thee: and the light shall shine upon thy ways.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
When men are cast down, then thou shalt say, There is lifting up; and he shall save the humble person.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”
He shall deliver the island of the innocent: and it is delivered by the pureness of thine hands.

< Yobu 22 >