< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
But Job answered and said,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hear diligently my speech, and let this be your consolations.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Suffer me that I may speak; and after that I have spoken, mock on.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
As for me, is my complaint to man? and if it were so, why should not my spirit be troubled?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Mark me, and be astonished, and lay your hand upon your mouth.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Even when I remember I am afraid, and trembling taketh hold on my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Wherefore do the wicked live, become old, yea, are mighty in power?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their seed is established in their sight with them, and their offspring before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are safe from fear, neither is the rod of Eloah upon them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bull gendereth, and faileth not; their cow calveth, and casteth not her calf.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock, and their children dance.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They take the timbrel and harp, and rejoice at the sound of the organ.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
They spend their days in wealth, and in a moment go down to the grave. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Therefore they say unto El, Depart from us; for we desire not the knowledge of thy ways.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
What is the Almighty, that we should serve him? and what profit should we have, if we pray unto him?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Lo, their good is not in their hand: the counsel of the wicked is far from me.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
How oft is the candle of the wicked put out! and how oft cometh their destruction upon them! Elohim distributeth sorrows in his anger.
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
They are as stubble before the wind, and as chaff that the storm carrieth away.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Eloah layeth up his iniquity for his children: he rewardeth him, and he shall know it.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
His eyes shall see his destruction, and he shall drink of the wrath of the Almighty.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what pleasure hath he in his house after him, when the number of his months is cut off in the midst?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Shall any teach El knowledge? seeing he judgeth those that are high.
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
One dieth in his full strength, being wholly at ease and quiet.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His breasts are full of milk, and his bones are moistened with marrow.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
And another dieth in the bitterness of his soul, and never eateth with pleasure.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
They shall lie down alike in the dust, and the worms shall cover them.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Behold, I know your thoughts, and the devices which ye wrongfully imagine against me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For ye say, Where is the house of the prince? and where are the dwelling places of the wicked?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Have ye not asked them that go by the way? and do ye not know their tokens,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
That the wicked is reserved to the day of destruction? they shall be brought forth to the day of wrath.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Who shall declare his way to his face? and who shall repay him what he hath done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Yet shall he be brought to the grave, and shall remain in the tomb.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
The clods of the valley shall be sweet unto him, and every man shall draw after him, as there are innumerable before him.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
How then comfort ye me in vain, seeing in your answers there remaineth falsehood?

< Yobu 21 >