< Yobu 13 >

1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
« Voici, mon œil a vu tout cela. Mon oreille l'a entendu et compris.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Ce que vous savez, je le sais aussi. Je ne suis pas inférieur à vous.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
« Certes, je parlerais au Tout-Puissant. Je désire raisonner avec Dieu.
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
Mais vous êtes des falsificateurs de mensonges. Vous êtes tous des médecins sans valeur.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
Oh, que vous soyez complètement silencieux! Alors vous seriez sage.
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Écoutez maintenant mon raisonnement. Écoutez les supplications de mes lèvres.
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
Parleras-tu injustement pour Dieu, et parler mensongèrement pour lui?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
Allez-vous faire preuve de partialité à son égard? Allez-vous lutter pour Dieu?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
Est-il bon qu'il te cherche? Ou comme on trompe un homme, le tromperez-vous?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
Il vous réprimandera sûrement si vous faites secrètement preuve de partialité.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Sa majesté ne vous fera-t-elle pas peur? et que son effroi s'abatte sur vous?
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Vos paroles mémorables sont des proverbes de cendre. Vos défenses sont des défenses d'argile.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
« Taisez-vous! Laissez-moi seul, que je puisse parler. Laisse venir sur moi ce qui va.
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
Pourquoi devrais-je prendre ma chair dans mes dents, et mettre ma vie dans ma main?
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Voici, il va me tuer. Je n'ai pas d'espoir. Néanmoins, je maintiendrai mes voies devant lui.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
C'est là aussi que sera mon salut, qu'un homme impie ne viendra pas devant lui.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Écoutez attentivement mon discours. Que ma déclaration soit dans vos oreilles.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
Voyez maintenant, j'ai mis ma cause en ordre. Je sais que je suis juste.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
Qui est celui qui contestera avec moi? Car alors je me tairais et abandonnerais l'esprit.
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
« Seulement, ne me fais pas deux choses, alors je ne me cacherai pas de ta face:
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
retire ta main loin de moi, et ne laisse pas ta terreur me faire peur.
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
Alors appelez, et je répondrai, ou laissez-moi parler, et vous me répondez.
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
Combien sont mes iniquités et mes péchés? Fais-moi connaître ma désobéissance et mon péché.
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
Pourquoi cachez-vous votre visage, et me considérer comme votre ennemi?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
Harcèlerez-vous une feuille morte? Allez-vous poursuivre le chaume sec?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
Car vous écrivez des choses amères contre moi, et me faire hériter des iniquités de ma jeunesse.
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
Tu as aussi mis mes pieds dans les ceps, et marque tous mes chemins. Tu as mis un lien à la plante de mes pieds,
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
bien que je me décompose comme une chose pourrie, comme un vêtement usé par les mites.

< Yobu 13 >