< Yobu 12 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Alors Job répondit,
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
« Sans doute, mais c'est vous qui êtes le peuple, et la sagesse mourra avec vous.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Mais j'ai de l'intelligence aussi bien que vous; Je ne suis pas inférieur à vous. Oui, qui ne connaît pas ce genre de choses?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Je suis comme celui qui se moque de son prochain, Moi, qui ai invoqué Dieu, et il m'a répondu. Le juste, l'homme irréprochable est une blague.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
Dans la pensée de celui qui est à l'aise, il y a du mépris pour le malheur. Il est prêt pour ceux dont le pied glisse.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Les tentes des brigands prospèrent. Ceux qui provoquent Dieu sont en sécurité, qui portent leur dieu dans leurs mains.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
« Mais demande maintenant aux animaux, et ils t'apprendront; les oiseaux du ciel, et ils vous le diront.
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Ou bien parle à la terre, et elle t'enseignera. Les poissons de la mer te déclareront.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Qui ne sait pas que dans tout cela, La main de Yahvé a fait cela,
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
dans la main duquel se trouve la vie de tout être vivant, et le souffle de toute l'humanité?
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
L'oreille n'essaie pas les mots, même lorsque le palais goûte sa nourriture?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Avec les hommes âgés se trouve la sagesse, dans la compréhension de la durée des jours.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
« La sagesse et la puissance sont auprès de Dieu. Il a le conseil et la compréhension.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Voici qu'il s'écroule, et il ne peut plus être reconstruit. Il emprisonne un homme, et il ne peut pas être libéré.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Voici, il retient les eaux, et elles tarissent. Encore une fois, il les envoie, et ils renversent la terre.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Avec lui, il y a la force et la sagesse. Le trompé et le trompeur sont à lui.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Il conduit les conseillers à l'écart, dépouillés. Il fait des juges des imbéciles.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Il délie les liens des rois. Il leur attache la taille avec une ceinture.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Il emmène les prêtres dépouillés, et renverse les puissants.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Il supprime la parole de ceux à qui l'on fait confiance, et enlève l'intelligence des anciens.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Il répand le mépris sur les princes, et détache la ceinture des forts.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Il découvre des choses profondes dans les ténèbres, et fait apparaître à la lumière l'ombre de la mort.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Il augmente les nations, et il les détruit. Il agrandit les nations, et il les conduit en captivité.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Il enlève l'intelligence aux chefs des peuples de la terre, et les fait errer dans un désert où il n'y a pas de chemin.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Ils tâtonnent dans l'obscurité, sans lumière. Il les fait tituber comme un homme ivre.