< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Så tog Job til Orde og svarede:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
"Ja, sandelig, I er de rette, med eder dør Visdommen ud!
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Også jeg har som I Forstand, står ikke tilbage for eder, hvo kender vel ikke sligt?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Til Latter for Venner er den, der råbte til Gud og fik Svar. den retfærdige er til Latter.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
I Ulykke falder de fromme, den sorgløse spotter Faren, hans Fod står fast, mens Fristen varer.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
I Fred er Voldsmænds Telte, og trygge er de, der vækker Guds Vrede, den, der fører Gud i sin Hånd.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Spørg dog Kvæget, det skal lære dig, Himlens Fugle, de skal oplyse dig,
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
se til Jorden, den skal lære dig lad Havets Fisk fortælle dig det!
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Hvem blandt dem alle ved vel ikke, at HERRENs Hånd har skabt det;
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
han holder alt levendes Sjæl i sin Hånd, alt Menneskekødets Ånd!
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Prøver ej Øret Ord, og smager ej Ganen Maden?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Er Alderdom eet med Visdom, Dagenes Række med Indsigt?
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Hos ham er der Visdom og Vælde, hos ham er der Råd og Indsigt.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Hvad han river ned, det bygges ej op, den, han lukker inde, kommer ej ud;
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
han dæmmer for Vandet, og Tørke kommer, han slipper det løs, og det omvælter Jorden.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Hos ham er der Kraft og Fasthed; den, der farer og fører vild, er hans Værk.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Rådsherrer fører han nøgne bort, og Dommere gør han til Tåber;
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
han løser, hvad Konger bandt, og binder dem Reb om Lænd;
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Præster fører han nøgne bort og styrter ældgamle Slægter;
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
han røver de dygtige Mælet og tager de gamles Sans;
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
han udøser Hån over Fyrster og løser de stærkes Bælte;
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
han drager det skjulte frem af Mørket og bringer Mulmet for Lyset,
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
gør Folkene store og lægger dem øde, udvider Folkeslags Grænser og fører dem atter bort;
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
han tager Jordens Høvdingers Vid og lader dem rave i vejløst Øde;
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
de famler i Mørke uden Lys og raver omkring som drukne.

< Yobu 12 >