< Yobu 10 >
1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
“Minha alma está cansada da minha vida. Darei livre curso à minha reclamação. Falarei com a amargura da minha alma.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Direi a Deus: 'Não me condenem'. Mostre-me por que você contende comigo.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
É bom para você que oprima, que você deve desprezar o trabalho de suas mãos, e sorrir para o conselho dos ímpios?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Você tem olhos de carne? Ou você vê como o homem vê?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
São seus dias como os dias dos mortais, ou seus anos como os anos do homem,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
que você inquirir após minha iniqüidade, e procurar por meu pecado?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Embora você saiba que eu não sou malvado, não há ninguém que possa entregar de sua mão.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
“'Suas mãos me incriminaram e me moldaram completamente, no entanto, vocês me destroem.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Lembre-se, eu lhe imploro, que você me moldou como barro. Você me trará de novo ao pó?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Você não me derramou como leite, e me coagulou como queijo?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Você me vestiu de pele e carne, e me unir com ossos e tendões.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Você me concedeu vida e bondade amorosa. Sua visitação preservou meu espírito.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
No entanto, você escondeu estas coisas em seu coração. Eu sei que isto é com você:
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
se eu pecar, então você me marca. Você não me absolverá de minha iniqüidade.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Se eu sou perverso, ai de mim. Se eu for justo, eu ainda não levantarei minha cabeça, estar cheio de vergonha, e consciente de minha aflição.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
Se minha cabeça está erguida, você me caça como um leão. Mais uma vez você se mostra poderoso para mim.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Você renova suas testemunhas contra mim, e aumente sua indignação comigo. As mudanças e a guerra estão comigo.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
“'Por que, então, você me trouxe para fora do útero? Gostaria de ter desistido do espírito, e nenhum olho me tinha visto.
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Eu deveria ter sido como se não tivesse sido. Eu deveria ter sido levado do útero para o túmulo.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Aren meus dias não são poucos? Pare! Deixe-me em paz, para que eu possa encontrar um pouco de conforto,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
antes de ir para onde eu não voltarei, para a terra das trevas e da sombra da morte;
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
a terra escura como a meia-noite, da sombra da morte, sem nenhuma ordem, onde a luz é como a meia-noite'”.