< Yobu 10 >
1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Naumaakon iti biagko; iyebkasko ti ririk; agsaoak iti kinasaem ti kararuak.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Ibagak ti Dios, 'Saannak laeng nga ukomen; ipakitam kaniak no apay nga ak-akusarannak.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Nasayaat kadi kenka a rumbeng nga idadanesnak, nga umsiem ti aramid dagiti imam kabayatan nga umis-isemka kadagiti panggep dagiti nadangkes?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Addaanka kadi kadagiti mata ti lasag? Makakitaka kadi a kas iti panagkita ti tao?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Dagiti aldawmo kadi ket kas iti al-aldaw dagiti sangkataoan wenno dagiti tawtawenmo kadi ket kas iti tawtawen dagiti tattao,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
nga agsaludsodka maipapan kadagiti kinadakesko ken sukimatem ti basolko,
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
uray no ammom nga awan basolko ken awan ti siasinoman a makaispal kaniak manipud iti imam?
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Siaannadnak a binukel ken sinukog dagiti imam, ngem daddadaelennak.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Lagipem, agpakaasiak kenka, a binukelnak a kasla pitak, isublinak kadi manen iti tapok?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Saan kadi nga imbukbuknak a kasla gatas ken binokelnak a kasla keso?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Kinawesannak iti kudil ken lasag ket pinagkakamangnak babaen kadagiti tulang ken piskel.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Inikkannak iti biag ken napudnoka iti tulagmo; binantayan ti tulongmo ti espirituk.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
Ngem inlemmengmo dagitoy a banbanag iti pusom—ammok a daytoy ti panpanunotem:
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
a no nagbasolak, maammoam daytoy; saannak a pakawanen iti kinadakesko.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
No nadangkesak, asiak pay; uray no nalintegak, saanko a maitangad ti ulok, agsipud ta napnoak iti pannakaibabain ken kumitkitaak iti bukodko a panagsagaba.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
No itangad ti ulok ti bukodna, anupennak a kasla leon; maminsan pay ipakitam kaniak a mannakabalinka unay.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Mangiy-iyegka kadagiti baro a saksi a maibusor kaniak ket nayunam ti pungtotmo a maibusor kaniak; darupennak babaen kadagiti baro nga armada.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Apay ngarud nga inruarnak manipud iti aanakan? Intedko la koman ti espirituk ket awan pulos ti mata a nakakita kaniak.
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Agbalinak koman a kasla saan nga imadda; naawitak la koman manipud iti tiyan agingga iti tanem.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Saan kadi a bassit laeng dagiti aldawko? Isardengmo ngaruden, bay-annak nga agmaymaysa, tapno makainanaak bassit
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
sakbay a mapanak iti lugar a saanakton nga agsubli, iti daga ti kinasipnget ken iti aniniwan ni patay,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
ti daga a nasipnget a kas iti kasipnget ti tengnga ti rabii, ti daga ti aniniwan ni patay, nga awan ti aniaman a urnosna, a ti lawag ket kasla tengnga ti rabii.”'