< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
My soul is disgusted with my life; I will give free vent to my complaint over myself; I will speak in the bitterness of my soul.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
I will say unto God, Do not condemn me; let me know for what cause thou contendest against me.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Is it well for thee that thou shouldst oppress, that thou shouldst reject the labor of thy hands, and shed light upon the counsel of the wicked?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Hast thou eyes of flesh? or wilt thou see as a mortal seeth?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Are thy days as the days of a mortal, or are thy years as the days of a man,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
That thou inquirest after my iniquity, and searchest after my sin?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Still it is within thy knowledge that I am not wicked, and there is none that can deliver me out of thy hand.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Thy hands have carefully fashioned me and made me; every thing is in harmony all round about; and yet thou dost destroy me!
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Remember, I beseech thee, that as though I were clay hast thou made me; and wilt thou cause me to return again unto the dust?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Behold, like milk didst thou pour me out, and like cheese didst thou curdle me.
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
With skin and flesh didst thou clothe me, and with bones and sinews didst thou cover me.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Life and kindness didst thou grant me, and thy providence watched over my spirit.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
And yet these things hadst thou treasured up in thy heart: I know that this was [resolved] within thee.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
If I have sinned, then dost thou watch me, and from my iniquity thou wilt not declare me guiltless.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
If I be wicked, woe unto me: and if I be righteous, I can still not lift up my head; I am sated with disgrace, and ever seeing my affliction;
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
And it constantly increaseth; like a fierce lion dost thou hunt for me; and again thou showest thyself continually wonderful on me;
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Thou ever renewest thy witnesses against me, and causest thy indignation to grow strong against me; changes and multitudes [of sufferings] are around me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Wherefore then didst thou bring me forth out of the womb? Oh that I had perished, and that no eye had seen me!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
That I were as though I had not been, —had been borne from the womb to the grave.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Lo! my days are but few: cease, then, withdraw from me [thy hand], that I may recover my cheerfulness a little.
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Before I go, and return not, to the land of darkness and the shadow of death,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
A land of utter gloom, as of the darkness of the shadow of death, without any order, and the light of which is like utter gloom.

< Yobu 10 >