< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Weary in my soul, I will pour my words with groans upon him: I will speak being straitened in the bitterness of my soul.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
And I will say to the Lord, Do not teach me to be impious; and therefore have you thus judged me?
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Is it good before you if I be unrighteous? for you have disowned the work of your hands, and attended to the counsel of the ungodly.
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Or do you see as a mortal sees? or will you look as a man sees?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Or is your life human, or your years [the years] of a man,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
that you have enquired into mine iniquity, and searched out my sins?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
For you know that I have not committed iniquity: but who is he that can deliver out of your hands?
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Your hands have formed me and made me; afterwards you did change [your mind], and strike me.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Remember that you have made me [as] clay, and you do turn me again to earth.
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Hast you not poured me out like milk, and curdled me like cheese?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
And you did clothe me with skin and flesh, and frame me with bones and sinews.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
And you did bestow upon me life and mercy, and your oversight has preserved my spirit.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
Having these things in yourself, I know that you can do all things; for nothing is impossible with you.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
And if I should sin, you watch me; and you have not cleared me from iniquity.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Or if I should be ungodly, woe is me: and if I should be righteous, I can’t lift myself up, for I am full of dishonor.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
For I am hunted like a lion for slaughter; for again you have changed and are terribly destroying me;
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
renewing against me my torture: and you have dealt with me in great anger, and you have brought trials upon me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Why then did you bring me out of the womb? and why did I not die, and no eye see me,
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
and I become as if I had not been? for why was I not carried from the womb to the grave?
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Is not the time of my life short? suffer me to rest a little,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
before I go whence I shall not return, to a land of darkness and gloominess;
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
to a land of perpetual darkness, where there is no light, neither [can any one] see the life of mortals.

< Yobu 10 >