< Yobu 10 >
1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
My soul is weary of my life, I will let go my speech against myself, I will speak in the bitterness of my soul.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
I will say to God: Do not condemn me: tell me why thou judgest me so.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Doth it seem good to thee that thou shouldst calumniate me, and oppress me, the work of thy own hands, and help the counsel of the wicked?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Hast thou eyes of flesh: or, shalt thou see as man seeth?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Are thy days as the days of man, and are thy years as the times of men:
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
That thou shouldst inquire after my iniquity, and search after my sin?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
And shouldst know that I have done no wicked thing, whereas there is no man that can deliver out of thy hand.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Thy hands have made me, and fashioned me wholly round about, and dost thou thus cast me down headlong on a sudden?
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Remember, I beseech thee, that thou hast made me as the clay, and thou wilt bring me into dust again.
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Hast thou not milked me as milk, and curdled me like cheese?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Thou hast clothed me with skin and flesh: thou hast put me together with bones and sinews:
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Thou hast granted me life and mercy, and thy visitation hath preserved my spirit.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
Although thou conceal these things in thy heart, yet I know that thou rememberest all things.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
If I have sinned and thou hast spared me for an hour: why dost thou not suffer me to be clean from my iniquity?
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
And if I be wicked, woe unto me: and if just, I shall not lift up my head, being filled with affliction and misery.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
And for pride thou wilt take me as a lioness, and returning thou tormentest me wonderfully.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Thou renewest thy witnesses against me, and multipliest thy wrath upon me, and pains war against me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Why didst thou bring me forth out of the womb: O that I had been consumed that eye might not see me!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
I should have been as if I had not been, carried from the womb to the grave.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Shall not the fewness of my days be ended shortly? suffer me, therefore, that I may lament my sorrow a little:
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Before I go, and return no more, to a land that is dark and covered with the mist of death:
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
A land of misery and darkness, where the shadow of death, and no order, but everlasting horror dwelleth.