< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
My soul is weary of my life. I will release my words against myself. I will speak in the bitterness of my soul.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
I will say to God: Do not be willing to condemn me. Reveal to me why you judge me this way.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Does it seem good to you, if you find fault with me and oppress me, the work of your own hands, and assist the counsel of the impious?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Do you have bodily eyes? Or, just as man sees, will you see?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Are your days just like the days of man, and are your years as the times of humans,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
so that you would inquire about my iniquity and examine my sin?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
And you know that I have done nothing impious, yet there is no one who can deliver from your hand.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Your hands have made me and formed me all around, and, in this way, do you suddenly throw me away?
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Remember, I ask you, that you have fashioned me like clay, and you will reduce me to dust.
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Have you not extracted me like milk and curdled me like cheese?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
You have clothed me with skin and flesh. You have put me together with bones and nerves.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
You have assigned to me life and mercy, and your visitation has preserved my spirit.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
Though you may conceal this in your heart, yet I know that you remember everything.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
If I have sinned, and you have spared me for an hour, why do you not endure me to be clean from my iniquity?
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
And if I should be impious, woe to me, and if I should be just, I will not lift up my head, being drenched with affliction and misery.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
And because of pride, you will seize me like a lioness, and having returned, you torment me to an extraordinary degree.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
You renew your testimony against me, and you multiply your wrath against me, and these punishments make war within me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Why did you lead me out of the womb? If only I had been consumed, so that no eye would ever see me!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
I should have been as if I had not been: transferred from the womb to the tomb.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Will not my few days be completed soon? Release me, therefore, so that I may lament my sorrows a little,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
before I depart and return no more to a land that is dark and covered with the fog of death,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
a land of misery and darkness, where the shadow of death, and nothing else but everlasting horror, dwells.

< Yobu 10 >