< Yobu 10 >
1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Душата ми се отегчи от живота ми; За това, ще се предам на оплакването си, Ще говоря в горестта на душата си.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Ще река Богу: Недей ме осъжда; Покажи ми защо ми ставаш противен.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Добре ли Ти е да оскърбяваш, И да презираш делото на ръцете Си, А да осветляваш съвещаното от нечестивите?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Телесни ли очи имаш? Или гледаш както гледа човек?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Твоите дни като дните на човека ли са, Или годините Ти като човешки дни,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
Та претърсваш беззаконието ми И издирваш греха ми,
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
При все че знаеш, че не съм нечестив, И че никой не може да ме избавя от ръката Ти?
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Твоите ръце ме създадоха и усъвършенствуваха Кръгло в едно; а пак съсипваш ли ме?
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Помни, моля, че като глина си ме създал; И в пръст ли ще ме възвърнеш?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Не си ли ме излял като мляко? Не си ли ме съсирил като сирене?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
С кожа и мускули си ме облякъл, И с кости и жили си ме оплел;
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Живот и благоволение си ми подарил, И провидението Ти е запазило духа ми.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
Но при все туй, това си криел в сърцето Си; Зная, че това е било в ума Ти;
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
Ако съгреша, наблюдаваш ме, И от беззаконието ми няма да ме считаш невинен,
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Ако съм нечестив, горко ми! И ако съм праведен, пак няма да дигна главата си. Пълен съм с позор; но гледай Ти скръбта ми,
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
Защото расте. Гониш ме като лъв, И повтаряш да се показваш страшен против мене.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Повтаряш да издигаш против мене свидетелите Си, И увеличаваш гнева Си върху мене; Едно подир друго войнства ме нападат.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Защо прочее ме извади Ти из утробата? Иначе, бих издъхнал без да ме е виждало око;
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Бих бил като че не съм бил; От утробата бих бил отнесен в гроба.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Дните ми не са ли малко? Престани, прочее, И остави ме да си отдъхна малко
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Преди да отида отдето няма да се върна, В тъмната земя и в смъртната сянка,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
Земя, мрачна като самата тъмнина, Земя на мрачна сянка и без никакъв ред, Дето виделото е като тъмнина.