< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
“O sons of Benjamin, be strengthened in the midst of Jerusalem, and sound the trumpet in Tekoa, and lift up a banner over the house of Haccherem. For an evil has been seen from the north, with great destruction.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
I have compared the daughter of Zion to a beautiful and delicate woman.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
The pastors will come to her with their flocks. They have pitched their tents against her all around. Each one will feed those who are under his hand.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
‘Sanctify a war against her! Rise up together, and let us ascend at midday.’ ‘Woe to us! For the day has declined; for the shadows of the evening have grown longer.’
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
‘Rise up, and let us ascend in the night, and let us destroy her houses.’”
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
For thus says the Lord of hosts: “Cut down her trees, and build a rampart around Jerusalem. This is the city of visitation! Every kind of false claim is in her midst.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
Just as a cistern makes its water cold, so has she made her wickedness cold. Iniquity and devastation will be heard in her; sickness and wounds will be ever before me.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
O Jerusalem, accept instruction, lest perhaps my soul may withdraw from you; lest perhaps I may set you in a desert, in an uninhabitable land.”
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
Thus says the Lord of hosts: “They will gather the remnant of Israel, even as a single cluster of grapes is gathered from a vine. Direct your hand, as a grape-gatherer directs his hand to the basket.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
To whom should I speak, and to whom should I testify, so as to be heard? Behold, their ears are uncircumcised, and so they are unable to hear. Behold, for them, the word of the Lord has become a disgrace. And so they will not accept it.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
For this reason, I have been filled with the fury of the Lord. I labor to bear it. Let it be poured out upon the child outside, or upon a group of young men meeting together. For a man will be taken captive with a woman, an elder will be taken captive with one who is full of days.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
And their houses will be given over to others, with both their lands and their wives. For I will extend my hand over the inhabitants of the earth, says the Lord.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
Certainly, from the least of them even to the greatest, all of them practice greed. And from the prophet even to the priest, all of them act with deceit.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
And they healed the destruction of the daughter of my people with disgrace, by saying: ‘Peace, peace.’ And there was no peace.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
They were confounded, because they committed an abomination. Or rather, they were not confounded with shame, because they did not know how to blush. For this reason, they will fall among those who are being destroyed. In the time of their visitation, they will fall, says the Lord.”
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Thus says the Lord: “Stand above the ways, and see and ask, about the ancient paths, as to which is the good way, and then walk in it. And you will find refreshment for your souls. But they said: ‘We will not walk.’
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
And I appointed watchers over you, saying: ‘Listen for the sound of the trumpet.’ And they said: ‘We will not listen.’
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
For this reason, hear, O Gentiles, and know, O congregation, how much I will do to them.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Hear, O earth! Behold, I will lead evils over this people, as the fruits of their own thoughts. For they have not listened to my words, and they have cast aside my law.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
For what reason are you bringing me frankincense from Sheba, and sweet smelling reeds from a far away land? Your holocausts are not acceptable, and your sacrifices are not pleasing to me.”
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Therefore, thus says the Lord: “Behold I will bring this people to utter ruin, and they will fall, with their fathers and sons; neighbor and relative will perish together.”
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
Thus says the Lord: “Behold, a people is coming from the land of the north, and a great nation will rise up from the ends of the earth.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
They will take hold of arrow and shield. They are cruel, and they will not take pity. Their voice will roar like the ocean. And they will climb upon horses, for they have been prepared like men for battle, against you, O daughter of Zion.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
‘We have heard of their fame. Our hands have become weakened. Tribulation has overtaken us, like the pains of a woman giving birth.’
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Do not choose to go out into the fields, and you should not walk along the roadway. For the sword and the terror of the enemy is on every side.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
Wrap yourself in haircloth, O daughter of my people. And sprinkle yourself with ashes. Make a mourning for yourself, as for an only son, a bitter lamentation: ‘for the destroyer will overwhelm us suddenly.’
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
I have presented you as a strong tester among my people. And you will test and know their way.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
All these leaders who are turning away and walking deceitfully, they are brass and iron; they have all been corrupted.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
The bellows has failed; the lead has been consumed by fire; the molten metal was melted to no purpose. For their wickedness has not been consumed.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Call them: ‘Rejected silver.’ For the Lord has cast them aside.”

< Yeremiya 6 >