< Maliro 1 >

1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
ALEPH. O how a city once filled with people now sits alone! The Governess of the Gentiles has become like a widow. The Prince of the provinces has been placed under tribute.
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
BETH. Weeping, she has wept through the night, and her tears are on her cheeks. There is no one to be a comfort to her and to all her beloved. All her friends have spurned her, and they have become her enemies.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
GHIMEL. Judah has migrated because of affliction and great servitude. She has lived among the nations and not found rest. All of her persecutors have apprehended her, amid torments.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
DALETH. The pathways of Zion mourn, because there are none who approach for the solemnity. All her gates are destroyed. Her priests groan. Her virgins are filthy. And she is overwhelmed with bitterness.
5 Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
HE. Her enemies have been made her leaders; her adversaries have been enriched. For the Lord has spoken against her, because of the multitude of her iniquities. Her little ones have been led into captivity before the face of the tribulator.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
VAU. And all her elegance has departed, from the daughter of Zion. Her leaders have become like rams that cannot find pasture, and they have gone away without strength before the face of the pursuer.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
ZAIN. Jerusalem has remembered the days of her affliction and the betrayal of all her desirable ones, whom she held from the days of antiquity, when her people fell into the hand of the enemy, and there was no one to be a helper. The enemies have looked upon her and mocked her Sabbaths.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
HETH. Jerusalem has sinned a grievous sinz. Because of this, she has become unstable. All who glorified her have spurned her, because they have looked upon her disgrace. Then she groaned and turned away again.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
TETH. Her filth is on her feet, and her end has not been remembered. She has been vehemently put down, having no consolation. O Lord, look upon my affliction, for the adversary has been lifted up.
10 Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
JOD. The enemy has sent his hand against all her desirable ones. For she has watched the Gentiles enter her sanctuary, even though you instructed that they should not enter into your church.
11 Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
CAPH. All her people are groaning and seeking bread. They have given up whatever was precious in exchange for food, so as to remain alive. See, O Lord, and consider, for I have become vile.
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
LAMED. O all you who pass by the way, attend, and see if there is any sorrow like my sorrow. For he has made me a vintage, just as the Lord has spoken in the day of his furious anger.
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
MEM. From on high, he has sent fire into my bones, and he has educated me. He has spread a net for my feet; he has turned me back. He has placed me in desolation, consumed by grief, all day long.
14 “Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
NUN. Vigilant is the yoke of my iniquities. They have been folded together in his hand and imposed on my neck. My virtue has been weakened. The Lord has given me into a hand, out of which I am not able to rise.
15 “Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
SAMECH. The Lord has taken away all of my great ones from my midst. He has called forth time against me, so as to crush my elect ones. The Lord has trampled the winepress, which was for the virgin daughter of Judah.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
AIN. For this I weep, and my eyes bring forth water. For the consoler has been far away from me, changing my soul. My sons have become lost, because the enemy has prevailed.
17 “Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
PHE. Zion has reached out her hands; there is no one to console her. The Lord has given orders against Jacob; his enemies are all around him. Jerusalem among them is like a woman made unclean by menstruation.
18 “Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
SADE. The Lord is just, for it is I who has provoked his mouth to wrath. I beg all people to listen and to see my sorrow. My virgins and my youths have gone into captivity.
19 “Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
COPH. I called for my friends, but they deceived me. My priests and my elders have been consumed in the city. For they were seeking their food, so as to revive their life.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
RES. See, O Lord, that I am in tribulation. My bowels have been disturbed, my heart has been subverted within me, for I am filled with bitterness. Outside, the sword puts to death, and at home there is a similar death.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
SIN. They have heard that I groan and that there is no one to console me. All my enemies have heard of my misfortune; they have rejoiced that you caused it. You have brought in a day of consolation, and so they shall become like me.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”
THAU. Let all their evil enter before you. And make vintage of them, just as you made vintage of me, because of all my iniquities. For my sighs are many, and my heart is grieving.

< Maliro 1 >