< Yeremiya 51 >

1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
Detta säger Herren: Si, jag skall uppväcka ett skarpt väder emot Babel, och emot hans inbyggare, som sig emot mig satt hafva.
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
Jag skall sända kastare till Babel, hvilka honom kasta skola, och utsopa hans land; desse skola vara allstädes omkring honom, på hans olyckos dag.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
Ty hans skyttar skola intet kunna skjuta, och hans väpnade skola intet kunna värja sig; så skoner nu intet hans unga män, gifver all hans här till spillo;
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
Så att de slagne ligga uti de Chaldeers land, och de genomstungne på hans gator.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
Ty Israel och Juda skola icke öfvergifne varda af Herranom Zebaoth, deras Gud, såsom enkor; ändock deras land hafver högeliga förbrutit sig uppå den Heliga i Israel.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
Flyr utaf Babel, på det hvar och en må undsätta sina själ, att I icke förgås uti hans ondsko; ty detta är Herrans hämndatid, och han vill betala honom.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Den gyldene kalken i Babel, som alla verldena hafver druckna gjort, är uti Herrans hand; alle Hedningar hafva druckit af hans vin, derföre äro Hedningarna så galne vordne.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
Huru hasteliga är Babel fallen och sönderslagen; jämrer eder öfver honom; tager ock salvo till hans sår, om han tilläfventyrs måtte helad varda.
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
Vi läke Babel; men han vill intet läkt varda; så låter nu fara honom, och låt oss hvar och en draga uti sitt land; ty hans straff räcker allt upp till himmelen, och sträcker sig upp till skyn.
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
Herren hafver framhaft våra rättfärdighet; kommer och låter oss förtälja Herrans vår Guds verk i Zion.
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
Ja, hvässer nu pilarna väl, och tillreder sköldarna. Herren hafver uppväckt Konungarnas mod i Meden; ty hans tankar stå emot Babel, att han skall förderfva honom; ty detta är Herrans hämnd, hans tempels hämnd.
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
Ja, reser nu baner upp på murarna i Babel, skicker vakt, sätter väktare, beställer håll; ty Herren tänker något, och skall desslikes fullfölja det han emot Babels inbyggare talat hafver.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
Du som vill stor vatten bor, och stora rikedomar hafver, din ände är kommen, och din girighet är ute;
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
Herren Zebaoth hafver svorit vid sina själ: Jag skall uppfylla dig med menniskor, likasom med gräsmatkar, de skola sjunga dig ena viso.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
Den som jordena, genom sin kraft, gjort hafver, och beredde verldenes krets genom sina vishet, och himmelen skickeliga utsträckte;
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Då han dundrar, så varder under himmelen mycket vatten, han uppdrager moln ifrå jordenes ända; han gör ljungeld i regnena, och låter vädret komma utu hemlig rum.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Alla menniskor äro dårar med sine konst, och alle guldsmeder bestå med skam med sin beläte; ty deras beläte äro bedrägeri, och hafva intet lif.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
De äro icke annat än fåfängelighet och förförisk verk; de måste förgås, då de hemsökte varda.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Men så är icke han, som Jacobs del är, utan han, som all ting gör, den äret, och Israel är hans arfs staf; Herren Zebaoth är hans Namn.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
Du äst min hammar och krigsvapen, genom dig skall jag slå folk och förderfva riken.
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
Jag skall slå dina hästar och resenärer, jag skall sönderslå dina vagnar och deras foromän;
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
Jag skall slå dina män och qvinnor; jag skall slå dina gamla och dina ynglingar; jag skall slå dräng och pigo;
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
Jag skall slå din herda och hjord; jag skall slå dina åkermän och ok; jag skall slå dina Förstar och herrar.
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
Ty jag vill vedergälla Babel, och allom Chaldeers inbyggarom, alla deras ondsko, som de uppå Zion bedrifvit hafva, för edor ögon, säger Herren.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
Si, jag skall till dig, du skadeliga berg, som hela verldena förderfvar, säger Herren; jag skall sträcka mina hand öfver dig, och välta dig neder af bergena, och göra ett förbrändt berg af dig;
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
Att man af dig hvarken hörnstenar eller grundstenar taga kan; utan ett evigt öde skall du vara, säger Herren.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
Reser upp baner i landena, blåser med basun ibland Hedningarna, ruster Hedningarna emot honom, kaller emot honom de Konungarike Ararat, Minni och Ascenas, beställer höfvitsmän emot honom, hafver hästar fram, likasom snorrande bromser.
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Ruster Hedningarna emot honom, nämliga Konungarna af Meden, samt med deras Förstar och herrar, och allt deras väldes land.
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
Och landet skall bäfva och förskräckas; förty Herrans tankar vilja fullkomnade varda emot Babel, att han gör Babels land till ett öde, der ingen uti bo skall.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
De hjeltar i Babel skola icke töra draga ut till strids, utan blifva på fästen; deras starkhet är borto, och äro vordne såsom qvinnor; hans boningar äro upptände, och hans bommar sönderbrutne.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
Här löper den ene om den andra, och det ena bådskapet möter thy andro, till att kungöra Konungenom i Babel, att hans stad vunnen är allt intill ändan;
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
Och hamnarna intagna, och sjöarna utbrände, och krigsfolket blödigt vordet.
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
Ty detta säger Herren Zebaoth, Israels Gud: Dottren Babel är såsom en tröskeloge, när man derpå tröskar; hennes skördeand varder snart kommandes.
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
NebucadNezar, Konungen i Babel, hafver uppfrätit mig, och omstört mig; han hafver gjort ett tomt käril af mig; han hafver uppslukat mig likasom en drake; han hafver fyllt sin buk af mine kräselighet; han hafver bortdrifvit mig.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
Men nu finner sig öfver Babel den arghet, som uppå mig och mitt kött bedrifven är, säger inbyggerskan i Zion; och mitt blod, öfver de inbyggare i Chaldeen, säger Jerusalem.
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Derföre säger Herren alltså: Si, jag skall uträtta dig dina sak, och hämnas dig; jag skall uttorka hans haf, och förtorka låta hans brunnar.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
Och Babel skall varda till en stenhop, och till en drakaboning, till ett vidunder, och till ett hvisslande, att der ingen uti bo skall.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
De skola allesamman ryta såsom lejon, och ropa likasom de unga lejon.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
Jag skall sätta dem med deras drickande uti hetta, och göra dem druckna, att de skola glade varda, och sofva en evig sömn, af hvilkom de aldrig uppvakna skola, säger Herren.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Jag skall nederföra dem likasom lamb, till att slagtas, såsom vädrar och bockar.
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
Huru är Sesach så vunnen, och den beprisade i allo verldene så intagen? Huru är Babel så till ett under vorden ibland Hedningarna?
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
Ett haf är gånget öfver Babel, och med dess många böljor är han öfvertäckt.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
Hans städer äro öfvergifne, och till ett torrt ödeland vordne; till ett land, der ingen uti bor, och der ingen menniska uti vandrar.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
Ty jag hafver hemsökt Bel i Babel, och rifvit utu hans hals det han uppsvulgit hade, och Hedningarna skola intet mer löpa till honom; ty murarna i Babel äro också nederfallne.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
Drager derut, mitt folk; hvar och en undsätte sina själ för Herrans grymma vrede.
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
Edor hjerta måtte eljest vek varda, och uppgifvas för det rykte, som man i landena höra skall; ty uti eno årena skall ett rykte gå, och sedan i andra årena också ett rykte om våld i landena, och en Förste skall vara emot den andra.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Derföre si, den tid kommer, att jag de afgudar i Babel hemsöka skall, och deras hela land till skam varda skall, och hans slagne derinne ligga skola.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
Himmel och jord, och hvad deruti är, skola glädja sig öfver Babel, att hans förstörare nordanefter komne äro, säger Herren.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
Och lika som Babel i Israel de slagna fällt hafver, alltså skola de slagne i Babel fällde varda uti hela landena.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
Så drager nu edar väg, I som svärdet undflytt hafven, och töfver icke länge; tänker uppå Herran uti fjerran land, och låter Jerusalem ligga eder i hjertat.
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
Vi vorom till skam komne, då vi den försmädelse höra måste, och skammen betäckte vår ansigte, då de främmande kommo öfver Herrans hus helgedom.
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
Derföre, si, den tid kommer, säger Herren att jag hans afgudar hemsöka skall, och i hela landena skola de dödssåre sucka.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
Och om Babel uppstege i himmelen och satte sina magt uti de höga fäste, så skola dock förstörare ifrå mig komma öfver honom, säger Herren.
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
Man hörer ena röst i Babel, och en stor jämmer i de Chaldeers land;
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
Ty Herren förderfvar Babel; han förderfvar honom med så stort skri och rumor, att hans böljor fräsa likasom stor vatten.
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
Ty förstöraren är kommen öfver Babel, hans hjeltar varda grepne, deras bågar varda sönderbrutne; ty hämndenes Gud, Herren, betalar honom.
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Jag skall göra hans Förstar, visa, herrar och höfvitsmän, och krigsmän druckna, så att de skola sofva en evig sömn, der de icke mer af uppvakna skola, säger Konungen, som heter Herren Zebaoth.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
Detta säger Herren Zebaoth: Murarna om den stora Babel skola undergrafne varda, och hans höga portar uppbrännas med eld, att Hedningarnas arbete skall fåfängt vara, och uppbrännas hvad folken med mödo uppbyggt hafva.
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
Detta är det ord, som Propheten Jeremia befallde SeraJa, Neria sone, Mahsea sons, då han med Zedekia, Juda Konung, drog till Babel, uti fjerde årena hans rikes. Och SeraJa var en fridsam Förste.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
Och Jeremia skref all den olycko, som öfver Babel komma skulle, uti ene bok, nämliga all denna orden, som emot Babel skrifne äro.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
Och Jeremia sade till SeraJa: Då du kommer till Babel, så se till och läs alla dessa orden;
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
Och säg: Herre, du hafver talat emot detta rummet, att du ville förderfva det, så att ingen skulle bo häruti, hvarken folk eller fä, utan vara till ett evigt öde.
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
Och när du hafver utläsit bokena, så bind en sten dervid, och kasta henne uti Phrath;
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
Och säg: Alltså skall Babel försänkt varda, och icke uppkomma igen, för den olycko, som jag skall öfver honom komma låta, utan förgås. Allt härtill hafver Jeremia talat.

< Yeremiya 51 >