< Ezekieli 29 >

1 Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
Uti tionde årena, på tolfte dagen i tionde månadenom, skedde Herrans ord till mig, och sade:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
Du menniskobarn, ställ ditt ansigte emot Pharao, Konungen i Egypten, och prophetera emot honom, och emot hela Egypti land.
3 Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
Predika, och säg: Detta säger Herren Herren: Si, jag vill till dig, Pharao, du Konung i Egypten, du store drake, som i vattnena ligger, och säger: Strömmen är min, och jag hafver gjort mig honom.
4 Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
Men jag skall lägga dig ett bett i munnen, och hänga fiskarna i dina floder vid din fjäll, och skall draga dig utu dinom ström, samt med alla fiskar i dina floder, som vid din fjäll hänga.
5 Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
Jag skall kasta dig med fiskarna bort utu din vatten, in uti öknena; du skall falla uppå markene, och intet igen upphemtad eller församlad varda, utan blifva djuromen på markene, och foglomen under himmelen, till ett as.
6 Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
Och alle de, som bo uti Egypten, skola förnimma att jag är Herren, derföre att de Israels huse en rörstaf voro;
7 Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
Hvilken, då de honom fattade, söndergick, och stack dem genom sidona; när de stödde sig vid honom, gick han sönder, och stack dem i ländena.
8 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
Derföre säger Herren Herren alltså: Si, jag vill låta svärdet komma öfver dig, och utrota i dig både folk och fä.
9 Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
Och Egypti land skall varda tomt och öde, och de skola förnimma, att jag är Herren; derföre, att han säger: Strömmen är min, och jag hafver gjort honom.
10 nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
Derföre, si, jag vill till dig, och till dina strömmar, och skall göra Egypti land tomt och öde, ifrå det tornet i Sevene, allt intill Ethiopiens gränsor.
11 Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
Att deruti hvarken fä eller folk gå eller bo skola, i fyratio år långt.
12 Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
Ty jag vill göra Egypti land öde, såsom dess öde gränsor, och låta dess städer öde ligga, såsom andra öde städer, i fyratio år långt; och skall förströ de Egyptier ibland Hedningarna, och förjaga dem bort i landen.
13 “‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
Dock detta säger Herren Herren: När de fyratio år ute äro, så skall jag åter samka de Egyptier tillhopa ifrå folken, dit de förströdde varda;
14 Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
Och skall omvända Egypti fängelse, och låta dem komma uti Patros land igen, det deras fädernesland är, och skola vara der ett fögo rike.
15 Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
Ty det skall vara litet emot annor rike, och intet mer rådandes vara öfver Hedningarna; och jag skall förminska dem, så att de intet råda skola öfver Hedningarna;
16 Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
Att Israels hus icke skall mer förlåta sig uppå dem, och synda dermed, att de hålla sig intill dem, och skola förnimma, att jag är Herren Herren.
17 Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
Och det begaf sig uti sjunde och tjugonde årena, på första dagenom i första månadenom, skedde Herrans ord till mig, och sade:
18 “Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
Du menniskobarn, NebucadNezar, Konungen i Babel, hafver fört sin här med stor mödo inför Tyrus, så att all hufvud voro skallot, och alle axlar försletne; och hans arbete är dock ännu honom eller hans här för Tyrus intet lönt vordet.
19 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
Derföre säger Herren Herren alltså: Si, jag skall gifva NebucadNezar, Konungen af Babel, Egypti land, att han skall taga bort allt dess gods, och skall skinna och beröfva det, på det han må gifva sinom här sold;
20 Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
Men Egypti land vill jag gifva honom för sitt arbete, som han derpå gjort hafver; ty de hafva tjent mig, säger Herren Herren.
21 “Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
På den tiden skall jag låta växa Israels hus horn, och skall upplåta din mun ibland dem, att de skola, förnimma att jag är Herren.

< Ezekieli 29 >