< Yeremiya 47 >

1 Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
Rijeè Gospodnja koja doðe Jeremiji proroku za Filisteje prije nego Faraon osvoji Gazu.
2 Yehova akuti, “Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto; adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo. Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo, mizinda ndi onse okhala mʼmenemo. Anthu adzafuwula; anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
Ovako veli Gospod: evo, voda dolazi sa sjevera, i biæe kao potok koji se razljeva, i potopiæe zemlju i što je u njoj, grad i one koji žive u njemu; i ljudi æe vikati, i ridaæe svi stanovnici zemaljski.
3 akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga, phokoso la magaleta ake ndi kulira kwa mikombero yake. Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo; manja awo adzangoti khoba.
Od topota kopita jakih konja njegovijeh, od tutnjave kola njegovijeh, i praske toèkova njegovijeh, neæe se obazreti ocevi na sinove, jer æe im ruke klonuti,
4 Pakuti tsiku lafika lowononga Afilisti onse ndi kupha onse otsala, onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni. Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti, otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
Od onoga dana koji æe doæi da istrijebi sve Filisteje i da zatre Tir i Sidon i sve ostale pomoænike, jer æe Gospod istrijebiti Filisteje, ostatak ostrva Kaftora.
5 Anthu a ku Gaza ameta mipala; anthu a ku Asikeloni akhala chete. Inu otsala a ku chigwa, mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
Oæelaviæe Gaza, propašæe Askalon i ostatak doline njihove; dokle æeš se rezati?
6 “Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova, kodi udzapumula liti? Bwerera mʼmalo ako; ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
Jaoh, maèu Gospodnji, kad æeš se smiriti? vrati se u korice svoje, stani i smiri se.
7 Koma lupangalo lidzapumula bwanji pamene Yehova walilamulira kuti lithire nkhondo Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”
Ali kako bi se smirio? jer mu Gospod dade zapovijest na Askalon i na primorje; onamo ga odredi.

< Yeremiya 47 >