< Yeremiya 42 >

1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
Tous les chefs de troupes, ainsi que Johanan, fils de Karèah, et Yaazania, fils de Hochaïa, et tout le peuple, grands et petits, s’avancèrent,
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
et dirent au prophète Jérémie: "Agrée, de grâce, notre supplication et implore l’Eternel, ton Dieu, pour nous, pour cette poignée des nôtres qui existent encore; car de nombreux que nous étions, nous sommes réduits à peu de chose, comme tes yeux s’en rendent compte en nous voyant.
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
Que l’Eternel, ton Dieu, nous indique le chemin que nous avons à suivre et la conduite que nous devons tenir!"
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
Le prophète Jérémie leur répondit: "Je vous entends; je vais implorer l’Eternel, votre Dieu, suivant votre demande, et toutes les réponses que l’Eternel m’adressera pour vous, je vous les communiquerai, sans rien vous cacher."
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
Et eux de répliquer à Jérémie: "Que l’Eternel se lève contre nous en témoin sincère et véridique, si nous manquons d’agir en tout conformément à ce que l’Eternel, ton Dieu, te donnera mission de nous dire!
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Que! a chose nous plaise ou nous déplaise, nous obéirons à la voix de l’Eternel, notre Dieu, auprès de qui nous te déléguons, avec la certitude d’être heureux par notre docilité aux ordres de l’Eternel, notre Dieu."
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
Au bout de dix jours, la parole de l’Eternel fut adressée à Jérémie.
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
Aussitôt il manda Johanan, fils de Karèah, et tous les chefs de troupes, ses compagnons, ainsi que le peuple tout entier, grands et petits,
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
et leur dit: "Voici ce qu’a déclaré l’Eternel, Dieu d’Israël, auprès de qui vous m’avez délégué pour lui exposer vos sollicitations.
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
Si vous continuez à demeurer dans ce pays, je vous y édifierai et ne vous détruirai pas, je vous y implanterai et ne vous en déracinerai plus; car j’ai regret au mal que je vous ai fait.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Ne redoutez pas le roi de Babylone, devant qui vous tremblez; non, ne le redoutez pas, dit l’Eternel, car je serai avec vous pour vous secourir et vous sauver de ses mains.
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
J’Attirerai sur vous sa compassion, il aura pitié de vous, et il vous rétablira sur votre territoire.
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
Mais si vous dites: "Nous ne voulons pas rester dans ce pays-ci," en refusant d’écouter la voix de l’Eternel, votre Dieu,
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
si vous dites: "Non pas! mais nous allons nous rendre en Egypte, où nous ne verrons plus de combats ni n’entendrons plus le son de la trompette ni ne souffrirons du manque de pain, et là nous nous établirons."
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
Eh bien donc! Ecoutez la parole de l’Eternel, ô survivants de Juda! Ainsi parle l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: Si réellement vous vous obstinez à vous rendre en Egypte, si vous y entrez pour y séjourner,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
il arrivera que le glaive dont vous avez peur vous y atteindra, dans ce pays d’Egypte, et la famine, objet de vos inquiétudes, elle s’attachera à vous dans cette Egypte, et vous y périrez.
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
Et tous les hommes qui se seront obstinés à pénétrer en Egypte pour y séjourner, ils deviendront la proie de l’épée, de la famine et de la peste, de sorte que personne parmi eux n’échappera et ne se soustraira au malheur que je ferai fondre sur eux.
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
Car ainsi parle l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: De même que ma colère et mon indignation se sont déversées sur les habitants de Jérusalem, de même mon courroux se déversera sur vous quand vous pénétrerez en Egypte. Vous deviendrez un objet d’imprécation, de stupeur, de malédiction et d’opprobre, et ne reverrez plus ce lieu-ci.
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
L’Eternel vous le dit, ô survivants de Juda: N’Allez pas en Egypte. Sachez bien que je vous avertis solennellement en ce jour.
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
Car vous vous êtes menti à vous-mêmes, lorsque vous m’avez délégué auprès de l’Eternel, votre Dieu, en disant: "Implore en notre faveur l’Eternel, notre Dieu, et tout ce que l’Eternel, notre Dieu, dira, rapporte-le nous fidèlement et nous agirons en conséquence."
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
Je vous ai tout rapporté en ce jour, mais vous n’écoutez pas la voix de l’Eternel, votre Dieu, et cela relativement à tout ce qu’il m’a donné mission de vous dire.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
Or donc, sachez-le bien, c’est par le glaive, par la famine et par la peste que vous périrez dans le pays où il vous plaît de vous rendre, pour y séjourner."

< Yeremiya 42 >