< Yeremiya 41 >

1 Pa mwezi wachisanu ndi chiwiri Ismaeli mwana wa Netaniya, mdzukulu wa Elisama amene anali wa banja laufumu ndiponso mmodzi wa atsogoleri a ankhondo a mfumu, anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ndi anthu khumi. Pamene ankadya naye kumeneko,
Dans le septième mois, Ismaël, fils de Netania, fils d’Elichama, qui était de race royale et un des hauts dignitaires du roi, arriva, accompagné de dix hommes, auprès de Ghedalia, fils d’Ahikam, à Miçpa; et là, à Miçpa, ils prirent part ensemble à un festin.
2 Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu khumi aja anayimirira ndi kupha ndi lupanga Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Choncho anapha munthu amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
Puis Ismaël, fils de Netania, et les dix hommes qui étaient avec lui se levèrent, frappèrent par le glaive Ghedalia, fils d’Ahikam, fils de Chafan, et le firent périr, lui que le roi de Babylone avait nommé gouverneur du pays.
3 Ismaeli anaphanso Ayuda onse amene anali pamodzi ndi Gedaliya ku Mizipa, kuphatikizanso asilikali a Ababuloni amene anali ku Mizipako.
De même tous les Judéens qui entouraient Ghedalia à Miçpa, ainsi que les Chaldéens qui s’y trouvaientles gens de guerre, Ismaël les massacra.
4 Mmawa mwake, anthu asanadziwe kuti Gedaliya waphedwa,
Le second jour, après le meurtre de Ghedalia, que personne encore ne connaissait,
5 kunafika anthu 80 ochekera ku Sekemu, Silo ndi Samariya, amene anali atameta ndevu zawo, atangʼamba zovala zawo ndi kudzichekacheka. Iwowa anatenga chopereka cha ufa ndi lubani kuti adzapereke ku Nyumba ya Yehova.
des hommes arrivèrent de Sichem, de Silo et de Samarie, au nombre de quatre-vingts, ayant la barbe rasée, les vêtements déchirés et le corps tailladé, portant dans leurs mains des offrandes et de l’encens qu’ils destinaient au temple de l’Eternel.
6 Ismaeli mwana wa Netaniya anachoka ku Mizipa akulira kupita kukakumana nawo. Atakumana nawo, iye anati, “Bwerani mudzaonane ndi Gedaliya mwana wa Ahikamu.”
lsmaël, fils de Netania, sortit de Miçpa pour aller à leur rencontre, en pleurant tout le long de la marche, et quand il fut auprès d’eux, il leur dit: "Venez trouver Ghedalia, fils d’Ahikam."
7 Atafika pakati pa mzinda, Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu amene anali naye anawapha anthuwo ndi kuwaponya mʼchitsime.
Mais dès qu’ils eurent pénétré dans l’intérieur de la ville, Ismaël, aidé des hommes qui étaient avec lui, les égorga et les jeta dans une citerne.
8 Koma anthu khumi a gululo anawuza Ismaeli kuti, “Musatiphe! Tili ndi tirigu ndi barele, mafuta ndi uchi, zimene tabisa mʼmunda.” Choncho anawasiya ndipo sanawaphere pamodzi ndi anzawo aja.
Parmi eux se trouvaient dix hommes qui dirent à Ismaël: "Ne nous fais pas mourir, car nous possédons des provisions cachées dans les champs, du froment, de l’orge, de l’huile et du miel." Il les épargna et ne les tua point comme leurs frères.
9 Tsono chitsime chimene anaponyamo mitembo ya anthu amene anawaphawo pamodzi ndi mtembo wa Gedaliya chinali chimene mfumu Asa anachikumba poopsedwa ndi Baasa mfumu ya Israeli. Ismaeli mwana wa Netaliya anachidzaza ndi mitembo.
Or, la citerne où Ismaël avait jeté les corps de tous les hommes qu’il avait frappés en même temps que Ghedalia, était celle que le roi Asa avait construite pour se défendre contre Baasa, roi d’Israël; c’est cette citerne qu’Ismaël, fils de Netania, remplit de cadavres.
10 Pambuyo pake Ismaeli anatenga ukapolo anthu ena onse amene anali ku Mizipa: ana aakazi a mfumu pamodzi ndi ena onse amene anatsalira kumeneko, amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anapatsa Gedaliya mwana wa Ahikamu kuti akhale bwanamkubwa wawo. Ismaeli mwana wa Netaliya anatenga ukapolo anthuwa ndi kuwoloka nawo kumapita ku dziko la Aamoni.
Et Ismaël fit main basse sur tout le reste de la population qui était à Miçpa, sur les princesses royales et l’ensemble des gens qui demeuraient a Miçpa et que Nebouzaradan, chef des gardes, avait placés sous l’autorité de Ghedalia, fils d’Ahikam. Ismaël, fils de Netania, les emmena tous comme prisonniers, et partit pour se rendre chez les Ammonites.
11 Pamene Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye pamodzi anamva zoyipa zonse zimene Ismaeli mwana wa Netaniya anachita,
Mais Johanan, fils de Karéah, et tous les commandants de troupes qui l’accompagnaient, ayant appris tout le mal fait par Ismaël, fils de Netania,
12 anatenga ankhondo awo onse kupita kukamenyana ndi Ismaeli mwana wa Netaniya. Anakamupeza kufupi ndi chidziwe chachikulu cha ku Gibiyoni.
ramassèrent tous leurs hommes, se mirent en route pour attaquer Ismaël, fils de Netania, et l’atteignirent près des grands étangs de Gabaon.
13 Pamene anthu onse amene Ismaeli anawagwira anaona Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali naye, anasangalala.
Quand tout le peuple qui se trouvait avec Ismaël aperçut Johanan, fils de Karéah, et tous les commandants de troupes qui l’accompagnaient, il fut dans la joie.
14 Anthu onse amene Ismaeli anawagwira ukapolo ku Mizipa anabwerera ndi kupita kwa Yohanani mwana wa Kareya.
Et tous les gens qu’Ismaël avait emmenés comme prisonniers de Miçpa firent volte face et, ayant changé de direction, se rallièrent à Johanan, fils de Karéah.
15 Koma Ismaeli pamodzi ndi anthu ake asanu ndi atatu, anathawa Yohanani ndi kuthawira kwa Aamoni.
Quant à Ismaël, fils de Netania, il se sauva avec huit hommes devant Johanan et se rendit auprès des Ammonites.
16 Kenaka Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye anatsogolera anthu onse otsala a ku Mizipa amene anawapulumutsa kwa Ismaeli mwana wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wa Ahikamu. Anthu amenewa anali: asilikali, akazi, ana ndi amuna ofulidwa otumikira mfumu amene anawatenga ku Gibiyoni.
Puis Johanan, fils de Karéah, et tous les chefs de troupes qui l’accompagnaient prirent tout le restant de la population qu’Ismaël, fils de Netania, avait enlevée de, Miçpa, après avoir assassiné Ghedalia, fils d’Ahikam: les adultes combattants, les femmes, les enfants et les eunuques qu’ils avaient ramenés de Gabaon.
17 Ndipo ananyamuka nayima ku Geruti Kimuhamu pafupi ndi Betelehemu pa ulendo wawo wopita ku Igupto
Ils se mirent en route et firent halte dans le cantonnement de Kimham, près de Bethléem, dans l’intention de partir de là et de se rendre en Egypte,
18 kuthawa Ababuloni. Iwo anaopa Ababuloniwo chifukwa Ismaeli mwana wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wa Ahikamu, amene mfumu ya ku Babuloni inamuyika kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
à cause des Chaldéens, dont ils avaient peur, parce qu’Ismaël, fils de Netania, avait mis à mort Ghedalia, fils d’Ahikam, établi comme gouverneur du pays par le roi de Babylone.

< Yeremiya 41 >