< Yeremiya 31 >

1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
Ngalesosikhathi, itsho iNkosi, ngizakuba nguNkulunkulu wensapho zonke zakoIsrayeli; bona-ke bazakuba ngabantu bami.
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
Itsho njalo iNkosi: Abantu babaseleyo benkemba bathola umusa enkangala; ngitsho uIsrayeli, lapho ngisiyamphumuza.
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
INkosi yabonakala kimi ikhatshana isithi: Yebo, ngikuthandile ngothando olulaphakade, ngakho-ke ngikudonsile ngothandolomusa.
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
Ngizabuya ngikwakhe, wakheke, wena ntombi emsulwa yakoIsrayeli; uzabuya uvunuliswe ngezigujana zakho, uphume phakathi kokugida kwabathokozayo.
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
Uzabuya uhlanyele izivini phezu kwezintaba zeSamariya; abahlanyeli bazahlanyela, badle izithelo.
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
Ngoba kuzakuba khona usuku abazamemeza ngalo abalindi entabeni yakoEfrayimi besithi: Sukumani, senyuke siye eZiyoni, eNkosini uNkulunkulu wethu.
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
Ngoba itsho njalo iNkosi: Mhlabeleleni uJakobe ngentokozo, limemezele phakathi kwenhloko yezizwe; zwakalisani, dumisani, lithi: Nkosi, sindisa abantu bakho, insali yakoIsrayeli.
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
Khangelani, ngizabaletha bevela elizweni lenyakatho, ngibabuthe emaceleni omhlaba; phakathi kwabo kukhona iziphofu labaqhulayo, abesifazana abakhulelweyo lababelethayo ndawonye; bazabuya lapha belibandla elikhulu.
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
Bazabuya belokukhala, ngizabakhokhela belokuncenga; ngizabahambisa emifuleni yamanzi ngendlela eqondileyo, abangayikukhubeka kuyo; ngoba nginguyise kaIsrayeli, loEfrayimi ulizibulo lami.
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
Zwanini ilizwi leNkosi, lina zizwe, lilimemeze ezihlengeni ezikhatshana, lithi: Yena owachitha uIsrayeli uzambutha, amgcine, njengomelusi umhlambi wakhe.
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
Ngoba iNkosi imhlengile uJakobe, yamhlawulela emsusa esandleni solamandla kulaye.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
Ngakho bazakuza bahlabelele ekuphakameni kweZiyoni, bagelezele kokuhle kweNkosi, ngamabele, langewayini elitsha, langamafutha, langamazinyane ezimvu, lenkomo; lomphefumulo wabo ube njengesivande esithelelweyo, kabasayikubuya babe losizi.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
Khona intombi izathokoza ekugideni, lamajaha labadala kanyekanye; ngoba ngizaphendula ukulila kwabo kube yintokozo, ngibaduduze, ngibathokozise, bangabi losizi.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
Njalo ngizasuthisa umphefumulo wabapristi ngamanono, labantu bami bazasuthiswa ngokuhle kwami, itsho iNkosi.
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
Itsho njalo iNkosi: Ilizwi lezwakala eRama, ukulila, ukukhala inyembezi okubuhlungu kakhulu; uRasheli ekhalela abantwana bakhe, esala ukududuzwa ngabantwana bakhe, ngoba bengasekho.
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
Itsho njalo iNkosi: Bamba ilizwi lakho ekukhaleni, lamehlo akho ezinyembezini; ngoba kulomvuzo womsebenzi wakho, itsho iNkosi, ngoba bazabuya bevela elizweni lesitha.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
Kukhona-ke ithemba enzalweni yakho, itsho iNkosi; ngoba abantwana bakho bazabuyela emngceleni wakibo.
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
Ngizwile lokuzwa uEfrayimi ezililelaesithi: Ungilayile, njalo ngalaywa njengethole elingathambanga; ngiphenduka, njalo ngizaphendula; ngoba uyiNkosi uNkulunkulu wami.
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
Isibili emva kokuphenduka kwami, ngazisola, lemva kokufundiswa kwami ngatshaya phezu kwethangazi lami; ngaba lenhloni, njalo ngayangeka, ngoba ngathwala ihlazo lobutsha bami.
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
UEfrayimi uyindodana yami eligugu yini, ungumntwana wami othokozisayo yini? Ngoba selokhu ngakhuluma ngimelene laye, ngisamkhumbula ngoqotho; ngenxa yalokho imibilini yami iyakhala ngaye; isibili ngizakuba lesihawu kuye, kutsho iNkosi.
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
Zibekele izitshengiso zendlela, uzimisele izinsika zeziqondiso, ubeke inhliziyo yakho kumgwaqo omkhulu, indlela owahamba ngayo; phenduka, ntombi emsulwa yakoIsrayeli, uphendukele kule imizi yakini.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
Koze kube nini uzulazula, ndodakazi ehlehlela nyovane? Ngoba iNkosi idale into entsha emhlabeni: Owesifazana uzahanqa indoda.
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
Itsho njalo iNkosi yamabandla, uNkulunkulu kaIsrayeli: Bazabuya batsho lelilizwi elizweni lakoJuda lemizini yakho, lapho ngibuyisela ukuthunjwa kwabo: Kwangathi iNkosi ingakubusisa, khaya lokulunga, ntaba yobungcwele.
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
Njalo kuzahlala kulo uJuda layo yonke imizi yakhe ndawonye, abalimi labahamba lemihlambi.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
Ngoba ngisuthise umphefumulo okhatheleyo, ngigcwalise wonke umphefumulo ophela amandla.
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
Ngasengiphaphama, ngabona; lobuthongo bami babumnandi kimi.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
Khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho ngizahlanyela indlu kaIsrayeli lendlu kaJuda ngenhlanyelo yabantu lenhlanyelo yenyamazana.
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
Kuzakuthi-ke njengalokho ngibalindile ukuthi ngisiphune lokuthi ngidilize lokuthi ngichithe lokuthi ngibhubhise lokuthi ngenze okubi, ngokunjalo ngizabalinda ukuze ngakhe ngihlanyele, itsho iNkosi.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
Ngalezonsuku kabasayikuthi: Oyise badlile izithelo zevini ezimunyu, amazinyo abantwana asetshelela.
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
Kodwa ngulowo lalowo uzafela ububi bakhe; wonke umuntu odla izithelo zevini ezimunyu, amazinyo akhe azatshelela.
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
Khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho ngizakwenza isivumelwano esitsha lendlu kaIsrayeli lendlu kaJuda;
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
kungeyisikho njengesivumelwano engasenza laboyise mhla ngibamba isandla sabo ukubakhupha elizweni leGibhithe, osivumelwano sami bona abasephulayo, lanxa mina ngangingumyeni wabo, itsho iNkosi.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
Kodwa yilesi isivumelwano engizasenza lendlu kaIsrayeli emva kwalezonsuku, itsho iNkosi: Ngizafaka umlayo wami emibilini yabo, ngiwubhale enhliziyweni yabo, ngibe nguNkulunkulu wabo, labo babe ngabantu bami.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
Kabasayikufundisa-ke, ngulowo lalowo umakhelwane wakhe, langulowo lalowo umfowabo, esithi: Yazi iNkosi; ngoba bonke bazangazi, kusukela komncinyane wabo kuze kufike komkhulu wabo, itsho iNkosi; ngoba ngizathethelela isiphambeko sabo, lesono sabo kangisayikusikhumbula.
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Itsho njalo iNkosi, enika ilanga libe yikukhanya emini, izimiso zenyanga lezezinkanyezi zibe yikukhanya ebusuku, enyakazisa ulwandle ukuze amagagasi alo ahlokome; iNkosi yamabandla libizo layo.
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
Uba lezozimiso zingasuka phambi kwami, itsho iNkosi, inzalo yakoIsrayeli layo izaphela ekubeni yisizwe phambi kwami zonke insuku.
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
Itsho njalo iNkosi: Uba engalinganiswa amazulu phezulu, zihlolwe izisekelo zomhlaba phansi, lami ngizayala yonke inzalo yakoIsrayeli ngenxa yakho konke abakwenzileyo, itsho iNkosi.
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
Khangela, insuku ziyeza, itsho iNkosi, lapho umuzi uzakwakhelwa iNkosi, kusukela emphotshongweni kaHananeli kuze kufike esangweni leNgonsi.
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
Lentambo yokulinganisa isezaphuma maqondana layo kuze kube soqaqeni lweGarebi, iphendukele ngaseGowa.
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
Lesihotsha sonke sezidumbu lesomlotha, lawo wonke amasimu kuze kufike esifuleni seKidroni, kuze kufike engonsini yeSango lamabhiza ngempumalanga, kuzakuba yibungcwele beNkosi. Kakuyikusitshunwa kakusayikudilizwa kuze kube nininini.

< Yeremiya 31 >