< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Så säger Herren: Himmelen är min stol, och jorden är min fotapall; hvad är det då för ett hus, som I mig bygga viljen? Eller hvar är det rummet, der jag hvila skall?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Min hand hafver gjort allt det som är, säger Herren; men jag ser till den elända, och till den som en förkrossad anda hafver, och till den som fruktar för mitt ord.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Ty den en oxa slagtar, är lika som han en man sloge; den ett får offrar, är såsom den der halsen sönderbröte af en hund; den spisoffer frambär, är såsom den der svinablod offrar; den som uppå rökelse tänker, han är såsom den det orätt är prisar; sådant utvälja de uti deras vägar, och deras själ hafver lust i deras styggelse.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Derföre vill jag ock utvälja det de tänka förvara sig före; det de frukta, vill jag låta kom öfver dem; derföre, att jag kallade, och ingen svarade; att jag talade, och de hörde intet, och gjorde det mig misshagade, och utvalde det mig icke täckt var.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Hörer Herrans ord, I som frukten för hans ord: Edre bröder, som eder hata, och afskilja eder för mitt Namns skull, säga: Låter se, huru härlig Herren är; låter se honom till edra glädje; de skola till skam varda.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
Ty man skall få höra en rumors röst i stadenom, en röst af templet; en Herrans röst, som sinom fiendom vedergäller.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Hon föder förr än hon får någon värk; förr än hennes nöd kommer, föder hon en pilt.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Ho hafver någon tid nu sådant hört? Ho hafver någon tid sådant sett? Kan ock, förr än ett land värk får, ett folk tillika födt varda? Nu hafver ju Zion födt sin barn utan värk.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Skulle jag andra låta öppna moderlifvet, och sjelf ock icke föda? säger Herren. Skulle jag Iåta andra föda, och sjelf tillyckt vara? säger din Gud.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Fröjder eder med Jerusalem, och varer glade öfver thy, alle I som det kärt hafven; fröjder eder med thy, alle I som deröfver sörjt hafven.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
Ty derföre skolen I suga, och mätte varda af dess hugsvalelses bröst; I skolen derföre suga, och lust hafva af dess härlighets fullhet.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Ty alltså säger Herren: Si, jag utbreder frid dervid såsom en ström, och Hedningarnas härlighet såsom en utsläppt bäck; då skolen I suga; I skolen i famna borne varda, och på knän skall man ljufliga hålla eder.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Jag vill hugsvala eder, såsom modren hugsvalar någon; ja, I skolen af Jerusalem lust hafva.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
I skolen få set, och edart hjerta skall glädja sig, och edor ben skola grönskas såsom gräs; då skall man känna Herrans hand på hans tjenare, och hans vrede på hans fiendar.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Ty si, Herren skall komma med eld, och hans vagnar såsom ett stormväder; att han skall vedergälla uti sine vredes grymhet, och hans straff uti en eldslåga.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Ty Herren skall döma igenom eld, och genom sitt svärd, allt kött, och de dräpne af Herranom skola vara månge.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
De som helga och rena sig i örtegårdar, den ene här, den andre der, och äta svinakött, styggelse och möss, skola tillsammans borttagne varda, säger Herren.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
Ty jag vill komma och församla deras gerningar och tankar, samt med alla Hedningar och tungomål, att de skola komma och se mina härlighet.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
Och jag vill gifva ett tecken ibland dem, och sända några af dem, som frälste äro, till Hedningarna vid hafvet; till Phul och Lud, till de bågaskyttar, till Thubal och Javan; och fjerran bort till de öar, der man intet af hört hafver, och de mina härlighet intet sett hafva; och skola förkunna mina härlighet ibland Hedningarna;
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
Och skola draga dertill alla edra bröder utaf allom Hedningom, Herranom till ett spisoffer, på hästar och på vagnar, på bårar, mular, på kärror, till Jerusalem, mitt helga berg, säger Herren, lika som Israels barn bära spisoffer i rena kärile, till Herrans hus.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
Och jag vill utaf de samma taga Prester och Leviter, säger Herren.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
Ty lika som den nye himmelen och den nya jorden, de jag skapar, stå för mig, säger Herren; alltså skall ock edor säd och namn stå.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
Och allt kött skall komma, den ena månaden efter den andra, och den ena Sabbathen efter den andra, till att tillbedja för mig, säger Herren.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
Och de skola gå ut, och se de menniskors kroppar; som emot mig misshandlat hafva; ty deras matk skall icke dö, och deras eld skall icke utslockna, och skola vara en styggelse för allt kött.

< Yesaya 66 >