< Ezara 8 >

1 Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
Desse äro hufvuden för deras fäder, som räknade vordo, och med mig uppdrogo ifrå Babel, i den tiden, då Konung Arthahsasta regerade.
2 Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
Af Pinehas barn: Gersom. Af Ithamars barn: Daniel. Af Davids barn: Hattus.
3 mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
Af Sechania barn, Paros barn: Zacharia, och med honom räknade hundrade och femtio män.
4 Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
Af PahathMoabs barn: Eljoenai, Seraja son, och med honom tuhundrad män.
5 Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
Af Sechania barn: Jahasiels son, och med honom trehundrad män.
6 Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
Af Adins barn: Ebed, Jonathans son, och med honom femtio män.
7 Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
Af Elams barn: Jesaia, Athalia son, och med honom sjutio män.
8 Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
Af Sephatja barn: Sebadja, Michaels son, och med honom åttatio män.
9 Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
Af Joabs barn: Obadja, Jehiels son, och med honom tuhundrad och aderton män.
10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
Af Selomiths barn: Josiphia son, och med honom hundrade och sextio män.
11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
Af Bebai barn: Zacharia, Bebai son, och med honom åtta och tjugu män.
12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
Af Asgads barn: Johanan, Katans son, och med honom hundrade och tio män.
13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
Af de sista Adonikams barn; och heto alltså: Eliphelet, Jehiel och Semaja, och med dem sextio män.
14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
Af Bigvai barn: Uthai och Sabbud, och med dem sjutio män.
15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
Och jag församlade dem till älfvena, som kommer till Ahava; och blefvom der i tre dagar. Och då jag gaf akt uppå folket och Presterna, fann jag der inga Leviter.
16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
Då sände jag till Elieser, Ariel, Semaja, Elnathan, Jarib, Elnathan, Nathan, Zacharia och Mesullam, öfverstar; och Jojarib och Elnathan, lärare;
17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
Och sände dem ut till Iddo öfverstan, till Casiphja, att de skulle hemta oss tjenare uti vår Guds hus. Och jag gaf dem in hvad de tala skulle med Iddo och hans bröder, de Nethinim i Casiphja.
18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
Och de hade till oss, efter Guds goda hand öfver oss, en klok man utaf Maheli barn, Levi sons, Israels sons, Serebia, med hans söner och bröder, aderton;
19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
Och Hasabia, och med honom Jesaia af Merari barn, med hans bröder och deras söner, tjugu;
20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
Och af de Nethinim, hvilka David och Förstarna gåfvo till att tjena Leviterna, tuhundrad och tjugu, alle nämnde vid namn.
21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Och jag lät der vid älfvena, vid Ahava, utropa ena fasto, att vi skulle ödmjuka oss för vårom Gud, till att söka af honom en rättan väg för oss, och vår barn, och alla våra håfvor.
22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
Ty jag skämdes bedas ledsagare och resenärar af Konungenom, att de skulle hjelpa oss för fienderna på vägenom; förty vi hade sagt Konungenom: Vår Guds hand är till det bästa öfver alla de honom söka; och hans starkhet och vrede öfver alla dem, som honom öfvergifva.
23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
Alltså fastade vi, och sökte detta af vårom Gud, och han hörde oss.
24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
Och jag afskiljde tolf af de öfversta Presterna, Serebia och Hasabia, och med dem tio deras bröder;
25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
Och vog dem till silfver, och guld, och tyg till häfoffer i vår Guds hus, hvilka Konungen, och hans rådherrar, och Förstar, och hele Israel, som för handene var, till häfoffer gifvit hade;
26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
Och vog dem till i deras hand sexhundrad och femtio centener silfver, och i silfvertyg hundrade centener, och i guld hundrade centener;
27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
Tjugu gyldene skålar, de höllo tusende gylden, och tu god kostelig kopparkäril, klar såsom guld;
28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
Och sade till dem: I ären helige Herranom; så äro ock kärilen helig; dertill det frigifna silfver och guld Herranom edra fäders Gud.
29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
Så vaker, och bevarer det, tilldess I vägen det inför öfversta Presterna, och Leviterna, och öfversta fäderna i Israel i Jerusalem, uti Herrans hus kistor.
30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
Då togo Presterna och Leviterna det vägna silfret, och guldet, och kärilen, att de skulle föra det till Jerusalem, till vår Guds hus.
31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
Alltså fore vi ifrån älfvene Ahava, på tolfte dagen i första månadenom, att vi skulle draga till Jerusalem; och vår Guds hand var öfver oss, och bevarade oss ifrå fiendernas hand och försåt på vägenom.
32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
Och vi komme till Jerusalem, och blefvom der i tre dagar.
33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
På fjerde dagenom vardt väget silfret och guldet, och kärilen uti vår Guds hus, under Meremoths hand, Uria sons Prestens, och med honom var Eleazar, Pinehas son; och med dem Josabath, Jesua son, och Noadja, Binnui son, de Leviter;
34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
Efter hvars tal och vigt; och vigten vardt på den tiden all beskrifven.
35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
Och fängelsens barn, som utu fängelset komne voro, offrade bränneoffer Israels Gudi, tolf stutar för hela Israel, sex och niotio vädrar, sju och sjutio lamb, tolf bockar till syndoffer; alltsammans till bränneoffer Herranom.
36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.
Och de antvardade Konungens befallning Konungens ämbetsmän och landshöfdingom på denne sidon älfven; och de upphöjde folket, och Guds hus.

< Ezara 8 >