< Yesaya 63 >

1 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
این کیست که از بصرهٔ ادوم می‌آید؟ این کیست که در لباسی باشکوه و سرخ رنگ، با قدرت و اقتدار گام بر زمین می‌نهد؟ «این منم، خداوند، که نجاتتان را اعلام می‌کنم! این منم که قدرت دارم نجات دهم.»
2 Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
چرا لباس او اینچنین سرخ است؟ مگر او در چرخشت، انگور زیر پای خود فشرده است؟
3 “Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
خداوند پاسخ می‌دهد: «بله، من به تنهایی انگور را در چرخشت، زیر پا فشردم. کسی نبود به من کمک کند. در غضب خود، دشمنانم را مانند انگور زیر پا له کردم. خون آنان بر لباسم پاشید و تمام لباسم را آلوده کرد.
4 Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
وقتش رسیده بود که انتقام قوم خود را بگیرم و ایشان را از چنگ دشمنان نجات دهم.
5 Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
نگاه کردم ببینم کسی به کمک من می‌آید، اما با کمال تعجب دیدم کسی نبود. پس، خشم من مرا یاری کرد و من به تنهایی پیروز شدم.
6 Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
با خشم خود قومها را زار و ناتوان کرده، آنها را پایمال نمودم و خونشان را به زمین ریختم.»
7 Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
از لطف و مهربانی خداوند سخن خواهم گفت و به سبب تمام کارهایی که برای ما کرده است او را ستایش خواهم کرد. او با محبت و رحمت بی‌حد خویش قوم اسرائیل را مورد لطف خود قرار داد.
8 Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
خداوند فرمود: «بنی‌اسرائیل قوم من هستند و به من خیانت نخواهند کرد.» او نجا‌ت‌دهندۀ ایشان شد
9 Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
و در تمامی رنجهای ایشان، او نیز رنج کشید، و فرشتۀ حضور وی ایشان را نجات داد. در محبت و رحمت خود ایشان را رهانید. سالهای سال ایشان را بلند کرد و حمل نمود.
10 Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
اما ایشان نافرمانی کرده، روح قدوس او را محزون ساختند. پس، او نیز دشمن ایشان شد و با آنان جنگید.
11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
آنگاه ایشان گذشته را به یاد آوردند که چگونه موسی قوم خود را از مصر بیرون آورد. پس، فریاد برآورده گفتند: «کجاست آن کسی که بنی‌اسرائیل را به رهبری موسی از میان دریا عبور داد؟ کجاست آن خدایی که روح قدوس خود را به میان قومش فرستاد؟
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
کجاست او که وقتی موسی دست خود را بلند کرد، با قدرت عظیم خود دریا را در برابر قوم اسرائیل شکافت و با این کار خود شهرت جاودانی پیدا کرد؟
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
چه کسی ایشان را در اعماق دریا رهبری کرد؟ آنان مانند اسبانی اصیل که در بیابان می‌دوند، هرگز نلغزیدند.
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
آنان مانند گله‌ای بودند که آرام در دره می‌چرند، زیرا روح خداوند به ایشان آرامش داده بود. «بله، تو قوم خود را رهبری کردی، و نام تو برای این کار شهرت یافت.»
15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
ای خداوند از آسمان به ما نگاه کن و از جایگاه باشکوه و مقدّست به ما نظر انداز. کجاست آن محبتی که در حق ما نشان می‌دادی؟ کجاست قدرت و رحمت و دلسوزی تو؟
16 Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
تو پدر ما هستی! حتی اگر ابراهیم و یعقوب نیز ما را فراموش کنند، تو ای یهوه، از ازل تا ابد پدر و نجا‌ت‌دهندۀ ما خواهی بود.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
خداوندا، چرا گذاشتی از راههای تو منحرف شویم؟ چرا دلهایی سخت به ما دادی تا از تو نترسیم؟ به خاطر بندگانت بازگرد! به خاطر قومت بازگرد!
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
ما، قوم مقدّس تو، مدت زمانی کوتاه مکان مقدّس تو را در تصرف خود داشتیم، اما اینک دشمنان ما آن را ویران کرده‌اند.
19 Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.
ای خداوند، چرا با ما طوری رفتار می‌کنی که گویا هرگز قوم تو نبوده‌ایم و تو نیز هرگز رهبر ما نبوده‌ای؟

< Yesaya 63 >