< Yesaya 58 >

1 “Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
„Стригэ ын гура маре, ну те опри! Ыналцэ-ць гласул ка о трымбицэ ши вестеште попорулуй Меу нелеӂюириле луй, касей луй Иаков пэкателе ей!
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Ын тоате зилеле Мэ ынтрябэ ши вор сэ афле кэиле Меле, ка ун ням каре ар фи ынфэптуит неприхэниря ши н-ар фи пэрэсит Леӂя Думнезеулуй сэу. Ымь чер хотэрырь дрепте, дореск сэ се апропие де Думнезеу.
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
‘Ла че не фолосеште сэ постим’, зик ей, ‘дакэ Ту ну везь? Ла че сэ не кинуим суфлетул, дакэ Ту ну ций сяма де лукрул ачеста?’ Пентру кэ”, зиче Домнул, „ын зиуа постулуй востру вэ лэсаць ын воя порнирилор воастре ши асуприць пе симбриаший воштри.
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Ятэ, постиць ка сэ вэ чоровэиць ши сэ вэ чертаць, ка сэ батець рэутэчос ку пумнул; ну постиць кум чере зиуа ачея, ка сэ ви се аудэ стригэтул сус.
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
Оаре ачеста есте постул плэкут Мие: сэ-шь кинуяскэ омул суфлетул о зи? Сэ-шь плече капул ка ун пипириг ши сэ се кулче пе сак ши ченушэ? Ачаста нумешть ту пост ши зи плэкутэ Домнулуй?
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
Ятэ постул плэкут Мие: дезлягэ ланцуриле рэутэций, дезноадэ легэтуриле робией, дэ друмул челор асуприць ши рупе орьче фел де жуг;
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
ымпарте-ць пыня ку чел флэмынд ши аду ын каса та пе ненорочиций фэрэ адэпост; дакэ везь пе ун ом гол, акоперэ-л ши ну ынтоарче спателе семенулуй тэу!
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Атунч лумина та ва рэсэри ка зориле ши виндекаря та ва ынколци репеде; неприхэниря та ыць ва мерӂе ынаинте ши слава Домнулуй те ва ынсоци.
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
Атунч ту вей кема, ши Домнул ва рэспунде, вей стрига, ши Ел ва зиче: ‘Ятэ-Мэ!’ Дакэ вей ындепэрта жугул дин мижлокул тэу, аменинцэриле ку деӂетул ши ворбеле де окарэ,
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
дакэ вей да мынкаря та челуй флэмынд, дакэ вей сэтура суфлетул липсит, атунч лумина та ва рэсэри песте ынтунечиме ши ынтунерикул тэу ва фи ка зиуа-н амяза маре!
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
Домнул те ва кэлэузи неынчетат, ыць ва сэтура суфлетул кяр ын локурь фэрэ апэ ши ва да дин ноу путере мэдуларелор тале; вей фи ка о грэдинэ бине удатэ, ка ун извор але кэруй апе ну сякэ.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
Ай тэй вор зиди ярэшь пе дэрымэтуриле де май ынаинте, вей ридика дин ноу темелииле стрэбуне; вей фи нумит
13 “Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
Дакэ ыць вей опри пичорул ын зиуа Сабатулуй, ка сэ ну-ць фачь густуриле тале ын зиуа Мя чя сфынтэ, дакэ Сабатул ва фи десфэтаря та, ка сэ сфинцешть пе Домнул, слэвинду-Л, ши дакэ-Л вей чинсти, неурмынд кэиле тале, неынделетничинду-те ку требуриле тале ши недедынду-те ла флекэрий,
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.
атунч те вей путя десфэта ын Домнул, ши Еу те вой суи пе ынэлцимиле цэрий, те вой фаче сэ те букурь де моштениря татэлуй тэу Иаков”, кэч гура Домнулуй а ворбит.

< Yesaya 58 >