< Yesaya 57 >

1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
Пере чел неприхэнит, ши нимэнуй ну-й пасэ; се дук оамений де бине, ши нимень ну я аминте кэ дин причина рэутэций есте луат чел неприхэнит.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
Ел интрэ ын паче ын гроапа луй: чел че умблэ пе друмул чел дрепт се одихнеште ын кулкушул луй.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
„Дар вой апропияци-вэ ынкоаче, фий ай врэжитоарей, сэмынца прякурварулуй ши а курвей!
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Де чине вэ батець вой жок? Ымпотрива куй вэ дескидець вой гура ларг ши скоатець лимба? Ну сунтець вой ниште копий ай пэкатулуй, о сэмынцэ а минчуний,
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
каре се ынкэлзеште пентру идоль суб орьче копак верде, каре ынжунгие пе копий ын вэй, суб крэпэтуриле стынчилор?
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Ын петреле луструите дин пырае есте партя та де моштенире, еле сунт соарта та; лор ле торнь ши жертфе де бэутурэ ши ле адучь дарурь де мынкаре. Пот Еу сэ фиу несимцитор ла лукрул ачеста?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Пе ун мунте ыналт ши ридикат ыць фачь кулкушул; тот аколо те суй сэ адучь жертфе.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
Ыць пуй помениря ын досул уший ши ушорилор, кэч, департе де Мине, ыць ридичь ынвелитоаря ши те суй ын пат, ыць лэрӂешть кулкушул ши фачь легэмынт ку ей; ыць плаче легэтура ку ей ши ей сяма ла семнул лор.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
Те дучь ла ымпэрат ку унтделемн, ыць ынмулцешть миресмеле, ыць тримиць солий департе ши те плечь пынэ ла Локуинца морцилор. (Sheol h7585)
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Обосешть мергынд ши ну зичь: ‘Ынчетез!’ Тот май гэсешть путере ын мына та, де ачея ну те добоарэ ынтристаря.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
Ши де чине те сфияй, де чине те темяй, де ну Мь-ай фост крединчоасэ, де ну ць-ай адус аминте ши ну ць-а пэсат де Мине? Ши Еу так, ши ынкэ де мултэ време, де ачея ну те темь ту де Мине.
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
Дар акум ыць вой да пе фацэ неприхэниря, ши фаптеле тале ну-ць вор фолоси!
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Ши атунч сэ стриӂь ши сэ те избэвяскэ мулцимя идолилор тэй! Кэч ый ва луа вынтул пе тоць, о суфларе ый ва ридика. Дар чел че се ынкреде ын Мине ва моштени цара ши ва стэпыни мунтеле Меу чел сфынт.”
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
Ши Ел зиче: „Кроиць, кроиць друм, прегэтиць каля, луаць орьче педикэ дин каля попорулуй Меу!”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
Кэч аша ворбеште Чел Пряыналт, а кэруй локуинцэ есте вешникэ ши ал кэруй Нуме есте сфынт: „Еу локуеск ын локурь ыналте ши ын сфинцение, дар сунт ку омул здробит ши смерит, ка сэ ынвиорез духуриле смерите ши сэ ымбэрбэтез инимиле здробите.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
Ну вряу сэ черт ын вечь, нич сэ цин о мыние некурматэ, кынд ынаинтя Мя кад ын лешин духуриле ши суфлетеле пе каре ле-ам фэкут.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Дин причина пэкатулуй лэкомией луй М-ам мыният ши л-ам ловит, М-ам аскунс, ын супэраря Мя, ши чел рэзврэтит а урмат ши май мулт пе кэиле инимий луй.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
Й-ам вэзут кэиле, ши тотушь ыл вой тэмэдуи; ыл вой кэлэузи ши-л вой мынгыя, пе ел ши пе чей че плынг ымпреунэ ку ел.
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
Вой пуне лауда пе бузе: Паче, паче челуй де департе ши челуй де апроапе!”, зиче Домнул. „Да, Еу ыл вой тэмэдуи!
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
Дар чей рэй сунт ка маря ынфуриятэ, каре ну се поате линишти ши але кэрей апе арункэ афарэ норой ши мыл.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Чей рэй н-ау паче”, зиче Думнезеул меу.

< Yesaya 57 >