< Yesaya 55 >

1 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Nuż wszyscy pragnący pójdźcie do wód, i wy, co niemacie pieniędzy, pójdźcie, kupujcie a jedzcie; pójdźcie, mówię, kupujcie bez pieniędzy i bez zapłaty, wino i mleko.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
Przecz wynakładacie pieniądze nie za chleb, a pracę swą na to, co nie nasyca? Słuchając słuchajcie mię, a jedzcie to, co jest dobrego, i niech się rozkocha w tłustości dusza wasza.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Nakłońcie ucha swego, a pójdźcie do mnie; słuchajcie, a będzie żyła dusza wasza. I postanowię z wami przymierze wieczne, miłosierdzie Dawidowe pewne wyleję na was.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Oto dałem go za świadka narodom, za wodza i za nauczyciela narodom.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
Oto naród, któregoś nie znał, powołasz, a narody, które cię nie znały, zbieżą się do ciebie dla Pana, Boga twego, i Świętego Izraelskiego; bo cię uwielbi.
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Szukajcie Pana, póki może być znaleziony; wzywajcie go, póki blisko jest.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
Niech opuści niepobożny drogę swoję, a człowiek nieprawy myśli swoje i niech się nawróci do Pana, a zmiłuje się; i do Boga naszego, gdyż jest hojnym w odpuszczaniu.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
Boć zaiste myśli moje nie są jako myśli wasze, ani drogi wasze jako drogi moje, mówi Pan;
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
Ale jako wyższe są niebiosa niż ziemia, tak przewyższają drogi moje drogi wasze, a myśli moje myśli wasze.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
Bo jako zstępuje deszcz i śnieg z nieba, a tam się więcej nie wraca, ale napawa ziemię, a czyni ją płodną, czyni ją też urodzajną, tak że wydaje nasienie siejącemu, a chleb jedzącemu:
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
Takci będzie słowo moje, które wynijdzie z ust moich; nie wróci się do mnie próżno, ale uczyni to, co mi się podoba, i poszczęści mu się w tem, na co je poślę.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
Przetoż w weselu wynijdziecie, a w pokoju doprowadzeni będziecie. Góry i pagórki chwałę przed wami głośno zaśpiewają, a wszystkie drzewa polne rękami klaskać będą.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”
Miasto ciernia wyrośnie jedlina, a miasto pokrzywy wyrośnie mirt; a to będzie Panu ku sławie, na znak wieczny, który nigdy nie będzie wygładzony.

< Yesaya 55 >