< Yesaya 57 >
1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
Sprawiedliwy ginie, a nikt tego do serca nieprzypuszcza; i mężowie pobożni schodzą, a nikt tego nie uważa, że przed przyjściem złego sprawiedliwy zebrany bywa;
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
Że wschodzi do pokoju, a odpoczywa na łożu swojem, ktokolwiek chodzi w uprzejmości.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
Ale wy sami przystąpcie, synowie czarownicy, nasienie cudzołożnika i wszetecznicy!
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Nad kimże się cieszycie? przeciwko komuż rozdzieracie gębę, i wywieszacie język? Izali nie jesteście synowie nierządu, nasienie kłamliwe?
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
Którzy nierząd płodzicie w gajach pod każdem drzewem zielonem zabijając synów swych przy potokach, pod wysokiemi skałami.
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Między gładkim kamieniem potokowym jest dział twój. Cić są, ci losem twoim, na które też wylewasz ofiarę mokrą, a ofiarujesz ofiarę śniedną, i w temże bym się Ja kochał?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Na górze wysokiej i wyniosłej postawiłeś łoże twoje, a tam wstępujesz ku sprawowaniu ofiar.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
A za drzwiami i za podwojem położyłaś pamiątkę twoję, gdyż odemnie odchodząc odkrywasz się, a wstąpiwszy rozszerzasz łoże swe, czyniąc je przestworniejsze, niżeli poganie; umiłowałaś łoże ich, gdziekolwiek miejsce upatrzysz.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol )
Chodzisz i do króla, z olejkiem i z rozmaitemi wonnemi maściami twemi; posyłasz bowiem posłów swych daleko, a poniżasz się aż do grobu. (Sheol )
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Mnóstwem dróg swoich spracowałaś się, a nie mówisz: Daremnać to. Znalazłaś pomoc ręce swojej, dlategoś nie zemdlała.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
Kogożeś się obawiała i lękała, iżeś kłamała? Na mięś nie pomniała, aniś tego przypuściła do serca swego: dlategoż to, żem Ja milczał, a to z dawna, nie boisz się mnie?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
Ja opowiem sprawiedliwość twoję i sprawy twoje, któreć nic nie pomogą.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Gdy zawołasz, niech cię wybawi zgraja twoja; ale wszystkie one rozniesie wiatr, i pochwyci marność. Lecz ten, co we mnie ufa, odziedziczy ziemię, a posiądzie górę świętą moję.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
Bo rzeką: Wyrównajcie, wyrównajcie, zgotujcie drogę, uprzątnijcie zawady z drogi ludu mojego.
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
Bo tak mówi on najdostojniejszy i najwyższy, który mieszka w wieczności, a święte jest imię jego: Ja, który mieszkam na wysokości na miejscu świętem, mieszkam i z tym, który jest skruszonego i uniżonego ducha, ożywiając ducha pokornych, ożywiając serce skruszonych.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
Nie będę się zaiste na wieki wadził, ani się wiecznie gniewał; boćby duch przed obliczem mojem zemdlał, i dusze, którem Ja uczynił.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Dla nieprawości łakomstwa jego rozgniewałem się, a uderzyłem go; ukryłem się, a rozgniewałem się, przeto, że odpornym będąc, poszedł drogą serca swego.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
Widzę drogi jego, wszakże uzdrowię go; doprowadzę go; i przywrócę mu pociechy, i tym, którzy z nim płaczą.
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
Stworzę owoc warg, pokój dalekiemu i bliskiemu, mówi Pan; a tak uzdrowię go.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
Lecz niepobożni będą jako morze wzburzone, gdy się uspokoić nie może, a którego wody wymiatają kał i błoto.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Niemasz pokoju niepobożnym, mówi Bóg mój.