< Yesaya 53 >
1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Кой е повярвал известието ни? И на кого се е открила мишцата Господна?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Защото израсна пред Него като отрасъл, И като корен от суха земя; Нямаше благоразумие, нито приличие та да Го гледаме, Нито красота та да Го желаем.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
Той бе презрян и отхвърлен от човеците. Човек на скърби и навикнал на печал; И, както човек, от когото отвръщат хората лице, Презрян бе, и за нищо Го не счетохме.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
Той наистина понесе печалта ни, И със скърбите ни се натовари; А ние Го счетохме за ударен, Поразен от Бога, и наскърбен.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Но Той биде наранен поради нашите престъпления, Бит биде поради нашите беззакония; На Него дойде наказанието дакарваще нашия мир, И с Неговите рани ние се изцелихме.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
Всички ние се заблудихме както овце, Отбихме се всеки от своя път; И Господ възложи на Него беззаконието на всички ни.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Той беше угнетяван, но смири Себе Си, И не отвори устата Си; Както агне водено на клане, И както овца, която пред стригачите си не издава глас, Така Той не отвори устата Си.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Чрез угнетителен съд биде грабнат; А кой от Неговия род разсъждаваше, Че биде отсечен отсред земята на живите Поради престъплението на Моите люде, върху които трябваше да падне ударът?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
И определиха гроба Му между злодеите, Но по смъртта Му при богатия; Защото не беше извършил неправда, Нито имаше измама в устата Му.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Но Господ благоволи той да бъде бит, предаде Го на печал; Когато направиш душата Му принос за грях, Ще види потомството, ще продължи дните Си, И това, в което Господ благоволи, ще успее в ръката Му.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
Ще види плодовете от труда на душата Си и ще се насити; Праведният Ми служител ще оправдае мнозина чрез знанието им за Него, И Той ще се натовари с беззаконията им
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Затова ще Му определя дял между великите, И Той ще раздели користи със силните, Защото изложи душата Си на смърт И към престъпници биде причислен, И защото взе на Себе Си греховете на мнозина И ходатайства за престъпниците.