< Yesaya 37 >
1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
А когато цар Езекия чу думите му, раздра дрехите си, покри се с вретище и влезе в Господния дом.
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
И прати управителя на двореца Елиаким, секретаря Шевна и старшите свещеници, покрити с вретища, при пророк Исаия Амосовия син.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
И рекоха му: Така казва Езекия: Ден на скръб, на изобличение и на оскърбление е тоя ден; защото настана часът да се родят децата, но няма сила за раждане.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
Може би Господ твоят Бог ще чуе думите на Рапсака, когото господарят му асирийският цар прати да укорява живия Бог и ще изобличи думите, които Господ твоят Бог чу, затова възнеси молба за остатъка що е оцелял.
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
И тъй, слугите на цар Езекия отидоха при Исаия.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
И Исаия им рече: Така да кажете на господаря си - така казва Господ: Не бой се от думите, които си чул, с които слугите на асирийския цар Ме похулиха.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Ето, аз ще туря в него такъв дух, щото, като чуе слух, ще се върне в своята земя; и ще го направя да падне от нож в своята земя.
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
И така, Рапсак, като се върна, намери, че асирийският цар воюваше против Ливна; защото бе чул, че той заминал от Лахис.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
И царят чу да казват за асирийския цар Тирак: Излезе да воюва против тебе. И когато чу това, прати посланици до Езекия, казвайки:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
Така да говорите на Юдовия цар Езекия, да речете: Твоят Бог, на Когото уповаваш, да те не мами като казва: Ерусалим няма да бъде предаден в ръката на асирийския цар.
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
Ето, ти чу какво направили всичките царе на всичките земи, как ги обрекли на изтребление: та ти ли ще се избавиш?
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
Боговете на народите избавиха ли ония, които бащите ми изтребиха, Гозан, Харан, Ресеф, и еденяните, които бяха в Таласар?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Где е ематският цар, арфадският цар и царете на града Сефаруим, на Ена и на Ава?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
А когато Езекия взе писмото от ръката на посланиците та го прочете, Езекия възлезе в Господния дом и го разгъна пред Господа.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
И Езекия се помоли пред Господа, като каза:
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Господи на Силите, Боже Израилев, Който седиш между херувимите, Ти и само Ти си Бог на всичките земни царства; Ти си направил небето и земята.
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
Приклони, Господи, ухото Си и чуй; отвори, Господи, очите Си и виж; и чуй всичките думи на Сенахирима, който изпрати тогова да похули живия Бог.
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
Наистина, Господи, асирийските царе запустиха всичките области и земите им;
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
и хвърлиха в огън боговете им, защото не бяха богове, но дело на човешки ръце, дървета и камъни; затова ги погубиха.
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
Сега, прочее, Господи Боже наш, отърви ни от ръката му, за да познаят всичките земни царства, че Ти си Господ, единственият Бог.
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
Тогава Исиая, Амосовият син, прати до Езекия да кажат: Така казва Господ Израилевият Бог: Чух това, за което си се помолил на Мене против асирийския цар Сенахирим.
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
Ето словото, което Господ изговори за него: Презря те, присмя ти се девицата, сионовата дъщеря: Зад гърба ти поклати глава Ерусалимската дъщеря.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
Кого си обидил и похулил ти? И против кого си говорил с висок глас И си надигнал нагоре очите си? Против светия Израилев.
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
Господа си обидил ти чрез слугите си, като си рекъл: С множеството на колесниците си възлязох аз Върху височината на планините, Върху уединенията на Ливан; И ще изсека високите му кедри, отбраните му елхи; И ще вляза в най-крайната му височина. В леса на неговия Кармил.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
Аз изкопах и пих вода: И със стъпалото на нозете си Ще пресуша всичките реки на Египет.
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Не си ли чул, че Аз съм наредил това отдавна. И от древни времена съм начертал това? А сега го изпълних. Така щото ти да обръщаш укрепени градове в купове развалини.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
Затова жителите им станаха безсилни, Уплашиха се и посрамиха се: Бяха като трева на полето, като зеленина, Като трева на къщния покрив. И жито препърлено преди да стане стъбло.
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
Но Аз зная жилището ти, Излизането ти и влизането ти, И буйството ти против Мене.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
Понеже буйството ти против Мене И надменността ти стигнаха до ушите Ми, Затова ще туря куката Си в ноздрите ти, И юздата Си в устата ти, Та ще те върна през пътя, по който си дошъл.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
И това ще ти бъде знамението: Тая година ще ядете това, което е саморасло. Втората година това, което израства от същото, А третата година посейте и пожънете Насадете лозя и яжте плода им.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
И оцелялото от Юдовия дом, Което е останало, пак ще пуска корени долу, И ще дава плод горе.
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
Защото из Ерусалим ще излезе остатък, И из хълма Сион оцелялото. Ревността на Господа на Силите ще извърши това.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
Затова, така казва Господ за асирийския цар - Няма да влезе в тоя град, Нито ще хвърли там стрела. Нито ще дойде пред него с щит, Нито ще издигне против него могила,
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
По пътя, през който е дошъл, по него ще се върне, И в тоя град няма да излезе, казва Господ;
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
Защото ще защитя тоя град за да го избавя, Заради Себе Си и заради слугата Ми Давида.
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
Тогава излезе ангел Господен та порази сто и осемдесет и пет хиляди души в асирийския стан; и когато станаха хора на сутринта, ето, всички ония бяха мъртви трупове.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
И тъй асирийският цар Сенахирим си тръгна та отиде, върна се, и живееше в Ниневия.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
А когато се кланяше в капището на бога си Нисрох, неговите синове Адрамелех и Сарасар, го убиха с нож; и побягнаха в Араратската земя. А вместо него се възцари син му Есарадон.