< Yesaya 46 >

1 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Bel has been broken. Nebo has been crushed. Their idols have been placed upon beasts and cattle, your grievous heavy burdens, even unto exhaustion.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
They have been melted down, or have been smashed together. They were not able to save the one who carried them, and their life will go into captivity.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
Listen to me, house of Jacob, all the remnant of the house of Israel, who are carried in my bosom, who were born from my womb.
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
Even to your old age, I am the same. And even with your grey hairs, I will carry you. I have made you, and I will sustain you. I will carry you, and I will save you.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
To whom would you liken me, or equate me, or compare me, or consider me to be similar?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
You take gold from a bag, and you weigh silver on a scale, so as to hire a goldsmith to make a god. And they fall prostrate and adore.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
They carry him on their shoulders, supporting him, and they set him in his place. And he will stand still and will not move from his place. But even when they will cry out to him, he will not hear. He will not save them from tribulation.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
Remember this, and be confounded. Return, you transgressors, to the heart.
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
Remember the past ages. For I am God, and there is no other god. There is no one like me.
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
From the beginning, I announce the last things, and from the start, the things that have not yet been done, saying: My plan will stand firm, and my entire will shall be done.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
I call a bird from the east, and from a far away land, the man of my will. And I have spoken it, and I will carry it out. I have created, and I will act.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
Hear me, you who are hard of heart, who are far from justice!
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
I have brought my justice near. It will not be far away, and my salvation will not be delayed. I will grant salvation in Zion, and my glory in Israel.

< Yesaya 46 >