< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Bride: May he kiss me with the kiss of his mouth. Groom to Bride: So much better than wine are your breasts,
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
fragranced with the finest perfumes. Bride to Groom: Your name is oil that has been poured out; therefore, the maidens have loved you.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Draw me forward. Chorus to Bride: We will run after you in the odor of your perfumes. Bride to Chorus: The king has led me into his storerooms. Chorus to Bride: We will exult and rejoice in you, remembering your breasts above wine. Groom to Bride: The righteous love you.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Bride to Chorus: O daughters of Jerusalem: I am black, but shapely, like the tabernacles of Kedar, like the tents of Solomon.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Do not be concerned that I am dark, for the sun has changed my color. The sons of my mother have fought against me. They have made me the keeper of the vineyards. My own vineyard I have not kept.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Bride to Groom: Reveal to me, you whom my soul loves, where you pasture, where you recline at midday, lest I begin to wander after the flocks of your companions.
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Groom to Bride: If you yourself do not know, O most beautiful among women, then go out and follow after the steps of the flocks, and pasture your young goats beside the tabernacles of the shepherds.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
O my love, I have compared you to my company of horsemen against the chariots of Pharaoh.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Your cheeks are beautiful, like those of a turtledove. Your neck is like a bejeweled collar.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Chorus to Bride: We will fashion for you chains of gold, accented with reddened silver.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Bride to Chorus: While the king was taking his rest, my aromatic ointment sent forth its odor.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
My beloved is a bundle of myrrh to me. He shall abide between my breasts.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
My beloved is a cluster of Cyprus grapes to me, in the vineyards of Engaddi.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Groom to Bride: Behold, you are beautiful, O my love. Behold, you are beautiful. Your eyes are those of a dove.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Bride to Groom: Behold, you are handsome, O my beloved, and graceful. Our bed is flourishing.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Groom to Bride: The timbers of our houses are of cedar; our ceilings are of cypress.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >