< Yesaya 41 >

1 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
Let the islands be silent before me, and let the nations take new strength. Let them draw near, and then speak. Let us apply for judgment together.
2 “Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
Who has raised up a just man from the east, and has called him to follow him? He will place the nations under his gaze, and he will rule over kings. He will cause them to be like dust before his sword, like chaff driven by the wind before his bow.
3 Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
He will pursue them. He will pass by in peace. No trace will appear after his feet.
4 Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
Who has worked and accomplished these things, calling to the generations from the beginning? “It is I, the Lord! I am the first and the last.”
5 Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
The islands saw it and were afraid. The ends of the earth were stupefied. They drew near and arrived.
6 aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
Each one will help his neighbor and will say to his brother, “Be strengthened.”
7 Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
The coppersmith striking with the mallet encouraged him who was forging at that time, saying, “It is ready for soldering.” And he strengthened it with nails, so that it would not be moved.
8 “Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
But you, O Israel, are my servant, O Jacob, whom I have chosen, the offspring of my friend Abraham.
9 Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
For his sake, I have taken you from the ends of the earth, and I have called you from its distant places. And I said to you: “You are my servant. I have chosen you, and I have not cast you aside.”
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
Do not be afraid, for I am with you. Do not turn away, for I am your God. I have strengthened you, and I have assisted you, and the right hand of my just one has upheld you.
11 “Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
Behold, all who fight against you shall be confounded and ashamed. They will be as if they did not exist, and the men who contradict you will perish.
12 Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
You will seek them, and you will not find them. The men who rebel against you will be as if they did not exist. And the men who make war against you will be like something that has been consumed.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
For I am the Lord your God. I take you by your hand, and I say to you: Do not be afraid. I have helped you.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
Fear not, O worm of Jacob, you who are dead within Israel. I have helped you, says the Lord, your Redeemer, the Holy One of Israel.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
I have established you like a new threshing cart, having serrated blades. You will thresh the mountains and crush them. And you will turn the hills into chaff.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
You will winnow them, and the wind will blow them away, and the whirlwind will scatter them. And you shall exult in the Lord; you shall rejoice in the Holy One of Israel.
17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
The indigent and the poor are seeking water, but there is none. Their tongue has been dried up by thirst. I, the Lord, will heed them. I, the God of Israel, will not abandon them.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
I will open rivers in the high hills, and fountains in the midst of the plains. I will turn the desert into pools of water, and the impassable land into streams of water.
19 Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
I will plant the cedar in a deserted place, with the thorn, and the myrtle, and the olive tree. In the desert, I will plant the pine, and the elm, and the box tree together,
20 kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
so that they may see and know, acknowledge and understand, together, that the hand of the Lord has accomplished this, and that the Holy One of Israel has created it.
21 “Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
Bring your case forward, says the Lord. Bring it here, if you have anything to allege, says the King of Jacob.
22 Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
Let them approach and announce to us the things that will occur. Announce to us the things that were before. And we will apply our heart to them, and we will know their end. And so, reveal to us the things that will occur.
23 tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
Announce the things that will occur in the future, and we will know that you are gods. Likewise, accomplish good or evil, if you are able, and let us speak of it and see it together.
24 Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
Behold, you exist out of nothing, and your work is from what does not exist; he who has chosen you is an abomination.
25 “Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
I have raised up one from the north, and he will arrive from the rising of the sun. He will call upon my name, and he will reduce magistrates to mud, like a potter working with clay.
26 Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
Who has announced this from its rising, so that we may know it, or from its beginning, so that we may say, “You are just.” There is no one who either announces, or predicts, or hears your words.
27 Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
The first one will say to Zion: “Behold, they are here,” and to Jerusalem, “I will present an evangelist.”
28 Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
And I saw, and there was no one among any of them to consult, or who, when I asked, could answer a word.
29 Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.
Behold, they are all unjust, and their works are empty. Their idols are wind and emptiness.

< Yesaya 41 >